8 Ndiyeno Mose anapitiriza kuti: “Yehova akakupatsani nyama yoti mudye madzulo ano ndi mkate wokwanira mʼmawa, muona kuti Yehova wamva kungʼungʼudza kwanu kotsutsana naye. Ife ndi ndani? Kungʼungʼudza kwanu si kotsutsana ndi ife, koma nʼkotsutsana ndi Yehova.”+