-
Deuteronomo 4:34Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
34 Kapena kodi Mulungu anayamba wapitapo kukatenga mtundu wa anthu kuti ukhale wake kuchokera pakati pa mtundu wina pogwiritsa ntchito ziweruzo,* zizindikiro, zodabwitsa,+ nkhondo,+ dzanja lamphamvu,+ mkono wotambasula komanso zinthu zoopsa+ zofanana ndi zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Iguputo inu mukuona?
-
-
Salimo 105:27-36Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
27 Iwowa anachita zizindikiro za Mulungu pamaso pa Aiguputo,
Anachita zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.+
31 Analamula kuti pagwe ntchentche zoluma,
Komanso tizilombo touluka toyamwa magazi,* mʼmadera awo onse.+
33 Anawononga mitengo yawo ya mpesa ndi ya mkuyu
Ndipo anakhadzula mitengo mʼdziko lawo.
35 Dzombelo linadya zomera zonse mʼdziko lawo,
Linadyanso mbewu zonse zamʼmunda mwawo.
-