Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 4:34
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Kapena kodi Mulungu anayamba wapitapo kukatenga mtundu wa anthu kuti ukhale wake kuchokera pakati pa mtundu wina pogwiritsa ntchito ziweruzo,* zizindikiro, zodabwitsa,+ nkhondo,+ dzanja lamphamvu,+ mkono wotambasula komanso zinthu zoopsa+ zofanana ndi zimene Yehova Mulungu wanu anakuchitirani ku Iguputo inu mukuona?

  • Nehemiya 9:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Ndiyeno munakhaulitsa Farao, atumiki ake onse ndiponso anthu onse amʼdziko lake powaonetsa zizindikiro ndi zodabwitsa.+ Munachita zimenezi chifukwa munadziwa kuti iwo anachita zinthu modzikuza+ kwa makolo athu. Pamenepa munadzipangira dzina lomwe lilipobe mpaka lero.+

  • Salimo 105:27-36
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Iwowa anachita zizindikiro za Mulungu pamaso pa Aiguputo,

      Anachita zodabwitsa zake mʼdziko la Hamu.+

      28 Mulungu anachititsa kuti mʼdziko la Iguputo mukhale mdima.+

      Iwo* sanapandukire mawu ake.

      29 Anasandutsa madzi a Aiguputo kukhala magazi,

      Ndipo anapha nsomba zawo.+

      30 Mʼdziko lawo munadzaza achule,+

      Ngakhalenso mʼzipinda za mafumu awo.

      31 Analamula kuti pagwe ntchentche zoluma,

      Komanso tizilombo touluka toyamwa magazi,* mʼmadera awo onse.+

      32 Anawagwetsera matalala mʼmalo mwa mvula,

      Anagwetsa mphezi* mʼdziko lawo.+

      33 Anawononga mitengo yawo ya mpesa ndi ya mkuyu

      Ndipo anakhadzula mitengo mʼdziko lawo.

      34 Analamula kuti pagwe dzombe,

      Dzombe lingʼonolingʼono losawerengeka.+

      35 Dzombelo linadya zomera zonse mʼdziko lawo,

      Linadyanso mbewu zonse zamʼmunda mwawo.

      36 Kenako Mulungu anapha mwana aliyense woyamba kubadwa mʼdziko lawo,+

      Chiyambi cha mphamvu zawo zobereka.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena