Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yobu 38:37
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 37 Ndi ndani amene ali wanzeru kwambiri moti angawerenge mitambo,

      Kapena ndi ndani amene angapendeketse zosungira madzi zakumwamba?+

  • Salimo 147:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  8 Imbirani amene amaphimba mapiri ndi mitambo,

      Amene amapereka mvula padziko lapansi,+

      Amenenso amameretsa udzu+ mʼmapiri.

  • Yeremiya 10:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Mawu ake akamveka,

      Madzi akumwamba amachita mkokomo,+

      Ndipo amachititsa mitambo* kukwera kuchokera kumalekezero a dziko lapansi.+

      Iye amachititsa kuti kukamagwa mvula mphezi zizingʼanima,

      Ndipo amatulutsa mphepo mʼnyumba zake zosungira.+

  • Amosi 9:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  6 ‘Amene amamanga makwerero ake kumwamba,

      Nʼkumanga nyumba yake pamwamba pa dziko lapansi.

      Ndiponso amasonkhanitsa madzi amʼnyanja

      Nʼkuwakhuthulira pansi,+

      Dzina lake ndi Yehova.’+

  • Mateyu 5:45
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 45 kuti musonyeze kuti ndinudi ana a Atate wanu wakumwamba.+ Chifukwa iye amawalitsira dzuwa lake anthu abwino ndi oipa omwe, ndipo amagwetsera mvula anthu olungama ndi osalungama omwe.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena