Salimo 2:8, 9 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 8 Tandipempha, ndipo ndikupatsa mitundu ya anthu kuti ikhale cholowa chako,Ndiponso dziko lonse lapansi kuti likhale lako.+ 9 Mitunduyo udzaiphwanya ndi ndodo yachifumu yachitsulo,+Ndipo udzaiswa ngati chiwiya chadothi.”+ Salimo 45:4, 5 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 4 Upite mu ulemerero wako ndipo upambane.*+Kwera pahatchi yako chifukwa cha choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo,+Ndipo dzanja lako lamanja lidzachita* zinthu zochititsa mantha. 5 Mivi yako ndi yakuthwa ndipo ikuchititsa kuti anthu agwe pamaso pako.+Imalasa mitima ya adani a mfumu.+ Mateyu 28:18 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 18 Tsopano Yesu anayandikira nʼkuwauza kuti: “Ulamuliro wonse waperekedwa kwa ine kumwamba ndi padziko lapansi.+ Chivumbulutso 6:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Nditayangʼana, ndinaona hatchi yoyera+ ndipo amene anakwera pahatchiyi ananyamula uta. Iye anapatsidwa chisoti chachifumu+ nʼkupita kukagonjetsa adani ake ndipo anapambana pankhondo yolimbana nawo.+ Chivumbulutso 12:5 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 5 Mkaziyo anabereka mwana wamwamuna,+ mnyamata amene adzakusa mitundu yonse ya anthu ndi ndodo yachitsulo.+ Ndipo mwana wakeyo anatengedwa msangamsanga nʼkupititsidwa kwa Mulungu ndi kumpando wake wachifumu. Chivumbulutso 19:11 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 Ndinaona kumwamba kutatseguka, kenako ndinaona hatchi yoyera.+ Amene anakwera pahatchiyo dzina lake linali lakuti Wokhulupirika+ ndi Woona.+ Iye amaweruza molungama ndipo akumenya nkhondo mwachilungamo.+ Chivumbulutso 19:15 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 15 Mʼkamwa mwake munkatuluka lupanga lalitali+ lakuthwa, loti aphere mitundu ya anthu ndipo adzawakusa ndi ndodo yachitsulo.+ Komanso iye ankapondaponda muchopondera mphesa cha mkwiyo waukulu wa Mulungu Wamphamvuyonse.+
8 Tandipempha, ndipo ndikupatsa mitundu ya anthu kuti ikhale cholowa chako,Ndiponso dziko lonse lapansi kuti likhale lako.+ 9 Mitunduyo udzaiphwanya ndi ndodo yachifumu yachitsulo,+Ndipo udzaiswa ngati chiwiya chadothi.”+
4 Upite mu ulemerero wako ndipo upambane.*+Kwera pahatchi yako chifukwa cha choonadi, kudzichepetsa ndi chilungamo,+Ndipo dzanja lako lamanja lidzachita* zinthu zochititsa mantha. 5 Mivi yako ndi yakuthwa ndipo ikuchititsa kuti anthu agwe pamaso pako.+Imalasa mitima ya adani a mfumu.+
18 Tsopano Yesu anayandikira nʼkuwauza kuti: “Ulamuliro wonse waperekedwa kwa ine kumwamba ndi padziko lapansi.+
2 Nditayangʼana, ndinaona hatchi yoyera+ ndipo amene anakwera pahatchiyi ananyamula uta. Iye anapatsidwa chisoti chachifumu+ nʼkupita kukagonjetsa adani ake ndipo anapambana pankhondo yolimbana nawo.+
5 Mkaziyo anabereka mwana wamwamuna,+ mnyamata amene adzakusa mitundu yonse ya anthu ndi ndodo yachitsulo.+ Ndipo mwana wakeyo anatengedwa msangamsanga nʼkupititsidwa kwa Mulungu ndi kumpando wake wachifumu.
11 Ndinaona kumwamba kutatseguka, kenako ndinaona hatchi yoyera.+ Amene anakwera pahatchiyo dzina lake linali lakuti Wokhulupirika+ ndi Woona.+ Iye amaweruza molungama ndipo akumenya nkhondo mwachilungamo.+
15 Mʼkamwa mwake munkatuluka lupanga lalitali+ lakuthwa, loti aphere mitundu ya anthu ndipo adzawakusa ndi ndodo yachitsulo.+ Komanso iye ankapondaponda muchopondera mphesa cha mkwiyo waukulu wa Mulungu Wamphamvuyonse.+