25 Choncho ophunzira enawo anamuuza kuti: “Ife tawaona Ambuye!” Koma iye anawayankha kuti: “Ndikapanda kuona mabala a misomali mʼmanja mwawo ndi kuika chala changa mʼmabala a misomaliwo ndiponso kuika dzanja langa munthiti mwawo,+ ndithu ine sindikhulupirira.”