6 Palibe aliyense amene angafanane ndi inu Yehova.+
Inu ndinu wamkulu ndipo dzina lanu ndi lalikulu komanso lamphamvu.
7 Kodi ndi ndani amene sakuyenera kukuopani, inu Mfumu ya mitundu yonse?+ Inuyo ndinu woyenera kuopedwa.
Chifukwa pakati pa anzeru onse a mʼmitundu ya anthu ndiponso pakati pa maufumu awo onse,
Palibiretu aliyense wofanana ndi inu.+