Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yeremiya 5:21
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 “Tamverani izi anthu opusa komanso opanda nzeru inu:*+

      Iwo ali ndi maso koma sangathe kuona,+

      Ali ndi makutu koma sangathe kumva.+

  • Mateyu 13:14, 15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Ulosi wa Yesaya ukukwaniritsidwa pa iwowa. Ulosiwo umanena kuti: ‘Kumva mudzamva ndithu, koma simudzazindikira tanthauzo lake. Kuyangʼana mudzangʼana ndithu, koma simudzaona chilichonse.+ 15 Chifukwa anthu awa aumitsa mitima yawo ndipo amva ndi makutu awo koma osalabadira. Atseka maso awo kuti asaone ndi maso awo komanso kuti asamve ndi makutu awo nʼkuzindikira tanthauzo lake mʼmitima yawo kenako nʼkutembenuka kuti ine ndiwachiritse.’+

  • Luka 8:9, 10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Koma ophunzira ake anamufunsa tanthauzo la fanizo limeneli.+ 10 Iye anati: “Inu mwapatsidwa mwayi woti mumvetse zinsinsi zopatulika za Ufumu wa Mulungu. Koma kwa enawo, zonse ndi mafanizo okhaokha.+ Izi zili choncho kuti kuyangʼana aziyangʼana ndithu, koma kukhale kopanda phindu, kumvanso azimva ndithu, koma asamamvetse zimene zikunenedwa.+

  • Machitidwe 28:25-27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 25 Choncho, popeza ankatsutsana, anayamba kuchoka. Koma Paulo ananena mawu awa:

      “Mzimu woyera unanena zoona kwa makolo anu kudzera mwa Yesaya mneneri. 26 Mzimuwo unati, ‘Pita ukauze anthu awa kuti: “Kumva mudzamva ndithu, koma simudzazindikira. Kuyangʼana mudzayangʼana ndithu, koma simudzaona chilichonse.+ 27 Chifukwa anthu awa aumitsa mitima yawo ndipo amva ndi makutu awo, koma osalabadira. Atseka maso awo kuti asaone ndi maso awo komanso kuti asamve ndi makutu awo nʼkumvetsa tanthauzo lake mʼmitima yawo, kenako nʼkutembenuka kuti ine ndiwachiritse.”’+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena