Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yeremiya 47:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 47 Yehova anauza mneneri Yeremiya mawu okhudza Afilisiti,+ Farao asanagonjetse mzinda wa Gaza.

  • Ezekieli 25:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Choncho Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, wanena kuti: “Ine ndikutambasula dzanja langa kuti ndilange Afilisiti,+ ndipo ndidzapha Akereti+ nʼkuwononga anthu onse omwe anatsala, amene amakhala mʼmbali mwa nyanja.+

  • Yoweli 3:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  4 Komanso kodi ndakulakwira chiyani

      Iwe Turo ndi Sidoni ndiponso nonse amʼchigawo cha Filisitiya?

      Kodi mukundichitira zimenezi pondibwezera zimene ndinachita?

      Ngati mukundibwezera,

      Ine ndidzakubwezerani mwamsanga ndiponso mofulumira zimene mwandichitirazo.+

  • Amosi 1:6-8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  6 Yehova wanena kuti,

      ‘“Chifukwa chakuti Gaza+ wandigalukira mobwerezabwereza, sindidzamusinthira chigamulo changa.

      Chifukwa anatenga anthu onse ogwidwa ukapolo+ nʼkuwapereka ku Edomu.

       7 Ndidzatumiza moto pampanda wa Gaza,+

      Ndipo udzawotcheratu nsanja zake zolimba.

       8 Ndidzapha anthu a ku Asidodi,+

      Komanso wolamulira* wa ku Asikeloni.+

      Ndidzalanga Ekironi,+

      Ndipo ndidzafafaniza Afilisiti otsala,”+ watero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.’

  • Zefaniya 2:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  4 Gaza adzakhala mzinda wosiyidwa,

      Ndipo Asikeloni adzakhala bwinja.+

      Anthu a ku Asidodi adzathamangitsidwa dzuwa likuswa mtengo,*

      Ndipo Ekironi adzazulidwa.+

  • Zekariya 9:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  5 Asikeloni adzaona zimenezi ndipo adzachita mantha.

      Gaza adzamva ululu waukulu.

      Izi zidzachitikiranso Ekironi chifukwa amene ankamudalira wachititsidwa manyazi.

      Ku Gaza sikudzakhalanso mfumu,

      Ndipo ku Asikeloni sikudzakhalanso anthu.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena