Yesaya 4:2 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 2 Tsiku limenelo, chinthu chimene Yehova adzachiphukitse chidzakhala chokongola komanso chaulemerero. Zipatso za mʼdzikolo zidzakhala zonyaditsa ndi zokongola kwa Aisiraeli amene adzapulumuke.+ Yesaya 27:6 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 6 Mʼmasiku amene akubwerawo, Yakobo adzamera mizu,Isiraeli adzaphuka nʼkuchita maluwa,+Ndipo iwo adzadzaza dzikolo ndi zipatso.+ Yesaya 35:6 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 6 Pa nthawi imeneyo, munthu wolumala adzadumpha ngati mmene imachitira mbawala,+Ndipo lilime la munthu wosalankhula lidzafuula mosangalala.+ Mʼchipululu mudzatumphuka madzi,Ndipo mʼdera lachipululu mudzayenda mitsinje. Yesaya 51:3 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 3 Chifukwa Yehova adzatonthoza Ziyoni.+ Iye adzatonthoza malo ake onse amene anawonongedwa.+Adzachititsa chipululu chake kukhala ngati Edeni+Ndipo dera lake lachipululu lidzakhala ngati munda wa Yehova.+ Mwa iye mudzakhala kusangalala ndi kukondwera,Kuyamikira ndi kuimba nyimbo zosangalatsa.+ Ezekieli 36:35 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 35 Anthu adzanena kuti: “Dziko limene linali bwinja tsopano lakhala ngati munda wa Edeni.+ Mizinda imene inawonongedwa ija, imene inali mabwinja ndiponso imene nyumba zake zinagwetsedwa, tsopano ili ndi mipanda yolimba kwambiri ndipo mukukhala anthu.”+
2 Tsiku limenelo, chinthu chimene Yehova adzachiphukitse chidzakhala chokongola komanso chaulemerero. Zipatso za mʼdzikolo zidzakhala zonyaditsa ndi zokongola kwa Aisiraeli amene adzapulumuke.+
6 Mʼmasiku amene akubwerawo, Yakobo adzamera mizu,Isiraeli adzaphuka nʼkuchita maluwa,+Ndipo iwo adzadzaza dzikolo ndi zipatso.+
6 Pa nthawi imeneyo, munthu wolumala adzadumpha ngati mmene imachitira mbawala,+Ndipo lilime la munthu wosalankhula lidzafuula mosangalala.+ Mʼchipululu mudzatumphuka madzi,Ndipo mʼdera lachipululu mudzayenda mitsinje.
3 Chifukwa Yehova adzatonthoza Ziyoni.+ Iye adzatonthoza malo ake onse amene anawonongedwa.+Adzachititsa chipululu chake kukhala ngati Edeni+Ndipo dera lake lachipululu lidzakhala ngati munda wa Yehova.+ Mwa iye mudzakhala kusangalala ndi kukondwera,Kuyamikira ndi kuimba nyimbo zosangalatsa.+
35 Anthu adzanena kuti: “Dziko limene linali bwinja tsopano lakhala ngati munda wa Edeni.+ Mizinda imene inawonongedwa ija, imene inali mabwinja ndiponso imene nyumba zake zinagwetsedwa, tsopano ili ndi mipanda yolimba kwambiri ndipo mukukhala anthu.”+