-
Yesaya 34:6Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
6 Yehova ali ndi lupanga. Lupangalo lidzakhala magazi okhaokha.
Lidzakhala mafuta okhaokha,+
Lidzakhala ndi magazi a nkhosa zamphongo zingʼonozingʼono komanso a mbuzi,
Lidzakhala ndi mafuta a impso za nkhosa zamphongo.
Chifukwa Yehova adzapereka nsembe ku Bozira,
Adzapha nyama zambiri mʼdziko la Edomu.+
-
-
Yesaya 63:1Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
63 Kodi amene akuchokera ku Edomuyu+ ndi ndani,
Amene akuchokera ku Bozira+ atavala zovala zowala zamitundu yosiyanasiyana,*
Amene zovala zake ndi zaulemelero,
Ndiponso amene akuyenda ndi mphamvu zake zochuluka?
“Ndine, amene ndikulankhula mwachilungamo,
Amene ndili ndi mphamvu zambiri zotha kupulumutsa.”
-