-
Yeremiya 29:31, 32Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
31 “Anthu onse amene ali ku ukapolo uwatumizire uthenga wakuti, ‘Ponena za Semaya wa ku Nehelamu, Yehova wanena kuti: “Popeza Semaya analosera kwa inu, ngakhale kuti ine sindinamutume ndipo anayesetsa kukuchititsani kuti mukhulupirire zinthu zabodza,+ 32 Yehova wanena kuti, ‘Ine ndilanga Semaya wa ku Nehelamu ndi mbadwa zake. Sipadzapezeka mwamuna aliyense wochokera mʼbanja lake amene adzapulumuke pakati pa anthu awa. Ndipo iye sadzaona zabwino zimene ndidzachitire anthu anga chifukwa walimbikitsa anthu kuti apandukire Yehova,’ akutero Yehova.”’”
-