Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 23:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Muzibweretsa kunyumba ya Yehova Mulungu wanu zipatso zoyamba kucha zamʼminda yanu zomwe ndi zabwino kwambiri.+

      Musamawiritse mwana wa mbuzi mumkaka wa mayi ake.+

  • Numeri 18:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Yehova anapitiriza kulankhula ndi Aroni kuti: “Ine ndakupatsa udindo woyangʼanira zinthu zonse zimene anthu azipereka kwa ine.+ Pa zinthu zonse zopatulika zimene Aisiraeli azipereka, ndakupatsa gawo iweyo ndi ana ako, kuti likhale lanu mpaka kalekale.+

  • Numeri 18:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Ndakupatsa+ mafuta onse abwino koposa, vinyo yense watsopano wabwino koposa ndi mbewu zabwino koposa, zimenezi ndi zipatso zawo zoyambirira+ zimene azipereka kwa Yehova.

  • Numeri 18:26, 27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 26 “Uza Alevi kuti, ‘Muzilandira kwa Aisiraeli chakhumi chimene ndakupatsani kuti chikhale cholowa chanu.+ Ndipo pa chakhumi chimene muzilandiracho, muzipereka chakhumi kwa Yehova.+ 27 Chakhumicho Mulungu azichiona kuti ndi chopereka chanu mofanana ndi tirigu wochokera pamalo opunthira,+ vinyo wochuluka wochokera mopondera mphesa kapena mafuta ochuluka ochokera mʼchofinyira mafuta.

  • Deuteronomo 18:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Aziperekanso kwa wansembe mbewu zawo zoyambirira kucha, vinyo wawo watsopano, mafuta awo ndi ubweya wa nkhosa zawo umene ameta moyambirira.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena