Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Yeremiya 18:7, 8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Nthawi iliyonse imene ndinganene kuti ndizula, kugwetsa ndi kuwononga mtundu uliwonse wa anthu kapena ufumu,+ 8 ndiyeno mtundu wa anthuwo nʼkusiya zoipa zimene ndinawadzudzula nazo, inenso ndidzasintha maganizo anga okhudza tsoka limene ndimafuna kuwagwetsera.+

  • Ezekieli 18:21-23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Koma ngati munthu woipa wasiya kuchita machimo ake onse amene ankachita ndipo akusunga malamulo anga nʼkumachita zinthu motsatira malamulo ndiponso mwachilungamo, ndithu iye adzapitiriza kukhala ndi moyo. Sadzafa ayi.+ 22 Iye sadzalangidwa chifukwa cha zolakwa zonse zimene anachita.*+ Adzapitiriza kukhala ndi moyo chifukwa chochita zinthu zolungama.’+

      23 ‘Kodi ine ndimasangalala ndi imfa ya munthu wochimwa?+ Kodi zimene ine ndimafuna si zoti munthu wochimwayo alape nʼkupitiriza kukhala ndi moyo?’+ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.

  • Yona 4:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Choncho iye anapemphera kwa Yehova kuti: “Inu Yehova, kodi zimene ndimaopa ndili kwathu zija si zimenezi? Nʼchifukwa chaketu ndinkafuna kuthawira ku Tarisi.+ Ndinadziwa kuti inu ndinu Mulungu wachifundo, wokoma mtima, wosakwiya msanga, wachikondi chokhulupirika chochuluka+ komanso mumamva chisoni mukafuna kubweretsa tsoka.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena