-
Ezekieli 18:21-23Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
21 Koma ngati munthu woipa wasiya kuchita machimo ake onse amene ankachita ndipo akusunga malamulo anga nʼkumachita zinthu motsatira malamulo ndiponso mwachilungamo, ndithu iye adzapitiriza kukhala ndi moyo. Sadzafa ayi.+ 22 Iye sadzalangidwa chifukwa cha zolakwa zonse zimene anachita.*+ Adzapitiriza kukhala ndi moyo chifukwa chochita zinthu zolungama.’+
23 ‘Kodi ine ndimasangalala ndi imfa ya munthu wochimwa?+ Kodi zimene ine ndimafuna si zoti munthu wochimwayo alape nʼkupitiriza kukhala ndi moyo?’+ akutero Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa.
-
-
Yona 4:2Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
2 Choncho iye anapemphera kwa Yehova kuti: “Inu Yehova, kodi zimene ndimaopa ndili kwathu zija si zimenezi? Nʼchifukwa chaketu ndinkafuna kuthawira ku Tarisi.+ Ndinadziwa kuti inu ndinu Mulungu wachifundo, wokoma mtima, wosakwiya msanga, wachikondi chokhulupirika chochuluka+ komanso mumamva chisoni mukafuna kubweretsa tsoka.
-