-
Luka 9:1-6Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
9 Kenako Yesu anasonkhanitsa atumwi 12 aja nʼkuwapatsa mphamvu ndi ulamuliro pa ziwanda zonse+ komanso kuti azitha kuchiritsa matenda.+ 2 Ndiyeno anawatumiza kuti azikalalikira za Ufumu wa Mulungu ndiponso kuchiritsa anthu. 3 Iye anawauza kuti: “Musatenge kanthu pa ulendowu, kaya ndodo, thumba la chakudya, mkate, ndalama kapena malaya awiri.*+ 4 Mukafika panyumba iliyonse, muzikhala mʼnyumbayo mpaka nthawi yochoka kumeneko itakwana.+ 5 Kulikonse kumene munthu sakakulandirani, mukamatuluka mumzinda umenewo muzisansa fumbi kumapazi anu kuti ukhale umboni wowatsutsa.”+ 6 Pamenepo ananyamuka nʼkulowa mʼderalo mudzi ndi mudzi nʼkumalengeza uthenga wabwino komanso kuchiritsa anthu kwina kulikonse.+
-