-
Mateyu 18:1-5Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
18 Pa nthawi imeneyo, ophunzira anabwera pafupi ndi Yesu nʼkumufunsa kuti: “Ndi ndani kwenikweni amene adzakhale wamkulu kwambiri mu Ufumu wakumwamba?”+ 2 Choncho iye anaitana mwana wamngʼono nʼkumuimika pakati pawo. 3 Kenako anawauza kuti: “Ndithu ndikukuuzani, mukapanda kutembenuka*+ nʼkukhala ngati ana aangʼono, simudzalowa mu Ufumu wakumwamba.+ 4 Choncho aliyense amene adzadzichepetse ngati mwana wamngʼonoyu ndi amene adzakhale wamkulu kwambiri mu Ufumu wakumwamba.+ 5 Ndiponso aliyense amene walandira mwana wamngʼono ngati ameneyu mʼdzina langa walandiranso ine.
-
-
Luka 9:46-48Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
46 Kenako iwo anayamba kukangana zokhudza amene anali wamkulu pakati pawo.+ 47 Yesu atazindikira zimene ankaganiza mumtima mwawo, anatenga mwana wamngʼono nʼkumuimika pambali pake. 48 Ndiyeno anawauza kuti: “Aliyense amene walandira mwana wamngʼono ngati uyu mʼdzina langa walandiranso ine. Ndipo aliyense amene walandira ine walandiranso amene anandituma.+ Chifukwa aliyense amene amachita zinthu ngati mwana wamngʼono pakati panu ndi amene ali wamkulu.”+
-