Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 18:1-5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Pa nthawi imeneyo, ophunzira anabwera pafupi ndi Yesu nʼkumufunsa kuti: “Ndi ndani kwenikweni amene adzakhale wamkulu kwambiri mu Ufumu wakumwamba?”+ 2 Choncho iye anaitana mwana wamngʼono nʼkumuimika pakati pawo. 3 Kenako anawauza kuti: “Ndithu ndikukuuzani, mukapanda kutembenuka*+ nʼkukhala ngati ana aangʼono, simudzalowa mu Ufumu wakumwamba.+ 4 Choncho aliyense amene adzadzichepetse ngati mwana wamngʼonoyu ndi amene adzakhale wamkulu kwambiri mu Ufumu wakumwamba.+ 5 Ndiponso aliyense amene walandira mwana wamngʼono ngati ameneyu mʼdzina langa walandiranso ine.

  • Luka 9:46-48
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 46 Kenako iwo anayamba kukangana zokhudza amene anali wamkulu pakati pawo.+ 47 Yesu atazindikira zimene ankaganiza mumtima mwawo, anatenga mwana wamngʼono nʼkumuimika pambali pake. 48 Ndiyeno anawauza kuti: “Aliyense amene walandira mwana wamngʼono ngati uyu mʼdzina langa walandiranso ine. Ndipo aliyense amene walandira ine walandiranso amene anandituma.+ Chifukwa aliyense amene amachita zinthu ngati mwana wamngʼono pakati panu ndi amene ali wamkulu.”+

  • Luka 22:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Kenako anayamba kukangana kwambiri za amene anali wamkulu kwambiri.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena