-
Mateyu 26:14-16Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
14 Kenako mmodzi wa ophunzira 12 aja, amene ankadziwika kuti Yudasi Isikariyoti,+ anapita kwa ansembe aakulu+ 15 nʼkuwafunsa kuti: “Kodi mudzandipatsa chiyani ndikamupereka kwa inu?”+ Iwo anamulonjeza ndalama 30 zasiliva.+ 16 Choncho kuyambira nthawi imeneyo anayesetsa kufunafuna mpata wabwino kuti amupereke.
-
-
Luka 22:3-6Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
3 Koma Satana analowa mwa Yudasi, amene ankadziwika kuti Isikariyoti, mmodzi wa ophunzira 12 aja.+ 4 Iye anapita kukakambirana ndi ansembe aakulu ndi oyangʼanira kachisi za mmene angamuperekere kwa iwo.+ 5 Iwo anasangalala ndipo anagwirizana kuti amupatse ndalama zasiliva.+ 6 Choncho iye anavomereza, ndipo anayamba kufunafuna mpata wabwino kuti amupereke kwa iwo popanda gulu la anthu pafupi.
-