Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 26:14-16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Kenako mmodzi wa ophunzira 12 aja, amene ankadziwika kuti Yudasi Isikariyoti,+ anapita kwa ansembe aakulu+ 15 nʼkuwafunsa kuti: “Kodi mudzandipatsa chiyani ndikamupereka kwa inu?”+ Iwo anamulonjeza ndalama 30 zasiliva.+ 16 Choncho kuyambira nthawi imeneyo anayesetsa kufunafuna mpata wabwino kuti amupereke.

  • Maliko 14:10, 11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Kenako Yudasi Isikariyoti, mmodzi wa ophunzira 12 aja, anachoka nʼkupita kwa ansembe aakulu kuti akapereke Yesu kwa iwo.+ 11 Atamva zimenezo, iwo anasangalala ndipo anamulonjeza kuti amupatsa ndalama zasiliva.+ Choncho iye anayamba kufunafuna mpata wabwino kuti amupereke.

  • Yohane 6:70
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 70 Yesu anawauza kuti: “Ine ndinakusankhani inu 12, si choncho?+ Komatu mmodzi wa inu ndi wonenera anzake zoipa.”*+

  • Yohane 13:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Chakudya chamadzulo chinali chili mkati ndipo Mdyerekezi anali ataika kale maganizo ofuna kupereka Yesu+ mumtima mwa Yudasi Isikariyoti,+ mwana wa Simoni.

  • Yohane 13:27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 27 Yudasi atalandira mkatewo, Satana analowa mwa iye.+ Choncho Yesu anamuuza kuti: “Zimene wakonza kuti uchite, zichite mwamsanga.”

  • Machitidwe 1:16, 17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 “Abale anga, zinali zofunika kuti lemba likwaniritsidwe, limene mzimu woyera unaneneratu kudzera mwa Davide. Lembali ndi lokhudza Yudasi,+ amene anatsogolera anthu okagwira Yesu.+ 17 Iye anali mmodzi wa ife,+ ndipo ankatumikira nafe limodzi.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena