Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Oweruza 14:5, 6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Choncho Samisoni anapita ku Timuna pamodzi ndi bambo ndi mayi ake. Atafika mʼminda ya mpesa ya ku Timuna, anakumana ndi mkango ndipo unayamba kubangula. 6 Ndiyeno mzimu wa Yehova unamupatsa mphamvu,+ moti anakhadzula mkangowo pakati ngati mmene munthu angakhadzulire kamwana ka mbuzi ndi manja. Koma sanauze bambo kapena mayi ake zimene anachitazi.

  • 1 Samueli 17:34-36
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 34 Davide anauza Sauli kuti: “Ine mtumiki wanu ndinakhala mʼbusa wa nkhosa za bambo anga. Ndiyeno kunabwera mkango+ komanso chimbalangondo ndipo chilombo chilichonse chinagwira nkhosa. 35 Zitatero, ndinatsatira chilombocho nʼkuchimenya, ndipo ndinapulumutsa nkhosa mʼkamwa mwake. Chitayamba kundilusira ndinachikoka ubweya* nʼkuchipha. 36 Ine mtumiki wanu ndinapha zilombo ziwiri zonsezi, mkango komanso chimbalangondo. Mfilisiti wosadulidwayu akhalanso ngati chimodzi mwa zilombo zimenezi, chifukwa wanyoza asilikali a Mulungu wamoyo.”+

  • Danieli 6:21, 22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 21 Nthawi yomweyo Danieli anayankha mfumuyo kuti: “Inu mfumu, mukhale ndi moyo mpaka kalekale. 22 Mulungu wanga watumiza mngelo wake kudzatseka pakamwa pa mikango+ moti sinandivulaze,+ chifukwa iye sanandipeze ndi mlandu uliwonse ndipo inunso mfumu sindinakulakwireni chilichonse.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena