Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 27
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Deuteronomo

      • Akalembe Chilamulo pamiyala (1-10)

      • Paphiri la Ebala ndi paphiri la Gerizimu (11-14)

      • Anatchulanso matemberero (15-26)

Deuteronomo 27:2

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “nʼkuipaka laimu woyera.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yos 8:30-32

Deuteronomo 27:3

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Nu 13:26, 27

Deuteronomo 27:4

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “mukaipake laimu woyera.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 11:29

Deuteronomo 27:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:25

Deuteronomo 27:7

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 3:1
  • +Le 7:15
  • +De 12:7

Deuteronomo 27:8

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 24:12

Deuteronomo 27:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 19:5; De 26:18

Deuteronomo 27:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +1Mf 2:3; Mt 19:17; 1Yo 5:3

Deuteronomo 27:12

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 11:29

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    2/1/1997, ptsa. 30-31

    6/15/1996, tsa. 14

Deuteronomo 27:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yos 8:33

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    2/1/1997, ptsa. 30-31

    6/15/1996, tsa. 14

Deuteronomo 27:14

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 33:10

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    6/15/1996, tsa. 14

Deuteronomo 27:15

Mawu a M'munsi

  • *

    Kapena kuti, “fano lachitsulo chosungunula nʼkulibisa.”

  • *

    Kapena kuti, “waluso pa ntchito za matabwa ndi zitsulo.”

  • *

    Kapena kuti, “Ame!” mʼChiheberi.

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:4; De 4:15, 16; Yes 44:9
  • +Eks 34:17; Le 19:4
  • +De 7:25; 29:17

Deuteronomo 27:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:12; De 21:18-21; Miy 20:20; 30:17; Mt 15:4

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    2/1/1997, ptsa. 30-31

Deuteronomo 27:17

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 19:14; Miy 23:10

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    2/1/1997, ptsa. 30-31

Deuteronomo 27:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 19:14

Deuteronomo 27:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 16:20; Miy 17:23; Mik 3:11
  • +Eks 22:21, 22; De 10:17, 18; Mki 3:5; Yak 1:27

Deuteronomo 27:20

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “wavula bambo ake.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 18:8; 1Ak 5:1

Deuteronomo 27:21

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 22:19; Le 18:23; 20:15

Deuteronomo 27:22

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 18:9; 20:17

Deuteronomo 27:23

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 18:17; 20:14

Deuteronomo 27:24

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 20:13; 21:12; Nu 35:31

Deuteronomo 27:25

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mt 27:3, 4

Deuteronomo 27:26

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 28:15; Aga 3:10

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 27:2Yos 8:30-32
Deut. 27:3Nu 13:26, 27
Deut. 27:4De 11:29
Deut. 27:5Eks 20:25
Deut. 27:7Le 3:1
Deut. 27:7Le 7:15
Deut. 27:7De 12:7
Deut. 27:8Eks 24:12
Deut. 27:9Eks 19:5; De 26:18
Deut. 27:101Mf 2:3; Mt 19:17; 1Yo 5:3
Deut. 27:12De 11:29
Deut. 27:13Yos 8:33
Deut. 27:14De 33:10
Deut. 27:15Eks 20:4; De 4:15, 16; Yes 44:9
Deut. 27:15Eks 34:17; Le 19:4
Deut. 27:15De 7:25; 29:17
Deut. 27:16Eks 20:12; De 21:18-21; Miy 20:20; 30:17; Mt 15:4
Deut. 27:17De 19:14; Miy 23:10
Deut. 27:18Le 19:14
Deut. 27:19De 16:20; Miy 17:23; Mik 3:11
Deut. 27:19Eks 22:21, 22; De 10:17, 18; Mki 3:5; Yak 1:27
Deut. 27:20Le 18:8; 1Ak 5:1
Deut. 27:21Eks 22:19; Le 18:23; 20:15
Deut. 27:22Le 18:9; 20:17
Deut. 27:23Le 18:17; 20:14
Deut. 27:24Eks 20:13; 21:12; Nu 35:31
Deut. 27:25Mt 27:3, 4
Deut. 27:26De 28:15; Aga 3:10
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 27:1-26

Deuteronomo

27 Ndiyeno Mose pamodzi ndi akulu a Isiraeli analamula anthuwo kuti: “Muzisunga lamulo lililonse limene ndikukupatsani lero. 2 Ndipo tsiku limene muwoloke Yorodano nʼkulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, mukaimike miyala ikuluikulu nʼkuipanga pulasitala.*+ 3 Kenako mukakawoloka, mukalembe pamiyalapo mawu onse a mʼChilamulo ichi, kuti mulowe mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, dziko loyenda mkaka ndi uchi, mogwirizana ndi zimene Yehova, Mulungu wa makolo anu anakulonjezani.+ 4 Mukawoloka Yorodano, mukaimike miyala imeneyi paphiri la Ebala,+ ndipo mukaipange pulasitala,* mogwirizana ndi zimene ndikukulamulani lero. 5 Komanso mukamangire Yehova Mulungu wanu guwa lansembe kumeneko, guwa lansembe lamiyala. Musakaseme miyalayo ndi chipangizo chilichonse chachitsulo.+ 6 Mukagwiritse ntchito miyala yathunthu pomangira Yehova Mulungu wanu guwa lansembe, ndipo mukapereke nsembe zopsereza kwa Yehova Mulungu wanu paguwalo. 7 Mukapereke nsembe zamgwirizano+ nʼkuzidyera pamenepo,+ ndipo mukasangalale pamaso pa Yehova Mulungu wanu.+ 8 Ndipo mukalembe moonekera bwino pamiyalayo mawu onse a mʼChilamulo chimenechi.”+

9 Kenako Mose komanso ansembe omwe ndi Alevi analankhula ndi Aisiraeli onse kuti: “Aisiraeli inu, khalani chete ndi kumvetsera. Lero mwakhala anthu a Yehova Mulungu wanu.+ 10 Muzimvera mawu a Yehova Mulungu wanu ndi kusunga malamulo+ ndi malangizo ake, amene ndikukupatsani lero.”

11 Tsiku limenelo Mose analamula anthuwo kuti: 12 “Mukawoloka Yorodano, mafuko otsatirawa ndi amene adzaimirire paphiri la Gerizimu+ nʼkudalitsa anthu: Fuko la Simiyoni, Levi, Yuda, Isakara, Yosefe ndi Benjamini. 13 Ndipo mafuko otsatirawa ndi amene adzaimirire paphiri la Ebala+ kuti azidzavomereza matemberero akamadzatchulidwa: Fuko la Rubeni, Gadi, Aseri, Zebuloni, Dani ndi Nafitali. 14 Ndipo Alevi azidzalankhula mokweza kwa anthu onse a mu Isiraeli kuti:+

15 ‘Wotembereredwa ndi munthu aliyense wopanga chifaniziro chosema+ kapena chifaniziro chachitsulo+ nʼkuchibisa.* Chifanizirocho, chomwe ndi ntchito ya manja a mmisiri waluso,* ndi chonyansa kwa Yehova.’+ (Anthu onse azidzayankha kuti, ‘Zikhale momwemo!’*)

16 ‘Wotembereredwa ndi munthu wonyoza bambo ake kapena mayi ake.’+ (Anthu onse azidzayankha kuti, ‘Zikhale momwemo!’)

17 ‘Wotembereredwa ndi munthu wosuntha chizindikiro cha malire a mnzake.’+ (Anthu onse azidzayankha kuti, ‘Zikhale momwemo!’)

18 ‘Wotembereredwa ndi munthu wosocheretsa munthu amene ali ndi vuto losaona.’+ (Anthu onse azidzayankha kuti, ‘Zikhale momwemo!’)

19 ‘Wotembereredwa ndi munthu wopotoza chiweruzo cha mlendo+ amene akukhala pakati panu, mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye.’+ (Anthu onse azidzayankha kuti, ‘Zikhale momwemo!’)

20 ‘Wotembereredwa ndi munthu wogona ndi mkazi wa bambo ake, chifukwa wachititsa manyazi bambo akewo.’*+ (Anthu onse azidzayankha kuti, ‘Zikhale momwemo!’)

21 ‘Wotembereredwa ndi munthu wogona ndi nyama iliyonse.’+ (Anthu onse azidzayankha kuti, ‘Zikhale momwemo!’)

22 ‘Wotembereredwa ndi munthu wogona ndi mchemwali wake, mwana wamkazi wa bambo ake kapena mwana wamkazi wa mayi ake.’+ (Anthu onse azidzayankha kuti, ‘Zikhale momwemo!’)

23 ‘Wotembereredwa ndi mwamuna wogona ndi apongozi ake.’+ (Anthu onse azidzayankha kuti, ‘Zikhale momwemo!’)

24 ‘Wotembereredwa ndi munthu wobisalira mnzake nʼkumupha.’+ (Anthu onse azidzayankha kuti, ‘Zikhale momwemo!’)

25 ‘Wotembereredwa ndi munthu wolandira chiphuphu kuti aphe munthu wosalakwa.’+ (Anthu onse azidzayankha kuti, ‘Zikhale momwemo!’)

26 ‘Wotembereredwa ndi munthu amene sadzatsatira mawu a mʼChilamulo ichi ndipo sadzawagwiritsa ntchito.’+ (Anthu onse azidzayankha kuti, ‘Zikhale momwemo!’”)

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena