Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 26
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Deuteronomo

      • Kupereka zipatso zoyambirira (1-11)

      • Chakhumi chachiwiri (12-15)

      • Aisiraeli anali chuma chapadera kwa Yehova (16-19)

Deuteronomo 26:2

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “zipatso.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 23:19; Le 23:10; Nu 18:8, 12; 2Mb 6:6; 31:5; Miy 3:9

Deuteronomo 26:3

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 17:1, 8; 26:3

Deuteronomo 26:5

Mawu a M'munsi

  • *

    Mabaibulo ena amati, “munthu wa Chiaramu amene watsala pangʼono kufa.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Ge 28:5; Ho 12:12
  • +Ge 46:3; Mac 7:15
  • +Ge 46:27
  • +Eks 1:7; De 10:22; Sl 105:24

Deuteronomo 26:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 1:11

Deuteronomo 26:7

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 3:9; 4:31; Mac 7:34

Deuteronomo 26:8

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 6:6
  • +Eks 7:3; De 4:33, 34

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    10/15/2015, ptsa. 4-5

Deuteronomo 26:9

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 3:8; De 8:7, 8; Eze 20:6

Deuteronomo 26:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 26:2

Deuteronomo 26:11

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 12:7; 16:14

Deuteronomo 26:12

Mawu a M'munsi

  • *

    Mʼchilankhulo choyambirira, “mʼmageti anu.”

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 12:5, 6; 14:22
  • +De 14:28, 29; Miy 14:21; 1Yo 3:17

Deuteronomo 26:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yak 1:27

Deuteronomo 26:14

Mawu a M'munsi

  • *

    Kutanthauza kukhala pa chisoni chifukwa cha imfa ya munthu amene ankamukonda.

Deuteronomo 26:15

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Eks 23:25
  • +De 8:7, 8
  • +Ge 15:18; 26:3

Deuteronomo 26:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 6:6; 11:1; Sl 119:34; 1Yo 5:3

Deuteronomo 26:17

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Le 26:46
  • +Mla 12:13
  • +Le 19:37

Deuteronomo 26:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 14:2; 29:10-13

Deuteronomo 26:19

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +De 4:8
  • +De 7:6; 28:1, 9

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Deut. 26:2Eks 23:19; Le 23:10; Nu 18:8, 12; 2Mb 6:6; 31:5; Miy 3:9
Deut. 26:3Ge 17:1, 8; 26:3
Deut. 26:5Ge 28:5; Ho 12:12
Deut. 26:5Ge 46:3; Mac 7:15
Deut. 26:5Ge 46:27
Deut. 26:5Eks 1:7; De 10:22; Sl 105:24
Deut. 26:6Eks 1:11
Deut. 26:7Eks 3:9; 4:31; Mac 7:34
Deut. 26:8Eks 6:6
Deut. 26:8Eks 7:3; De 4:33, 34
Deut. 26:9Eks 3:8; De 8:7, 8; Eze 20:6
Deut. 26:10De 26:2
Deut. 26:11De 12:7; 16:14
Deut. 26:12De 12:5, 6; 14:22
Deut. 26:12De 14:28, 29; Miy 14:21; 1Yo 3:17
Deut. 26:13Yak 1:27
Deut. 26:15Eks 23:25
Deut. 26:15De 8:7, 8
Deut. 26:15Ge 15:18; 26:3
Deut. 26:16De 6:6; 11:1; Sl 119:34; 1Yo 5:3
Deut. 26:17Le 26:46
Deut. 26:17Mla 12:13
Deut. 26:17Le 19:37
Deut. 26:18De 14:2; 29:10-13
Deut. 26:19De 4:8
Deut. 26:19De 7:6; 28:1, 9
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Deuteronomo 26:1-19

Deuteronomo

26 “Mukakalowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti likhale cholowa chanu, ndipo mukakalitengadi nʼkumakhalamo, 2 mukatenge zina mwa zipatso zoyambirira pa zokolola* zonse zamʼmunda mwanu zimene mudzakolole mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Mukaziike mʼdengu nʼkupita nazo kumalo amene Yehova Mulungu wanu adzasankhe kuika dzina lake.+ 3 Muzikapita kwa wansembe amene azidzatumikira masiku amenewo nʼkumuuza kuti, ‘Lero ndikuvomereza pamaso pa Yehova Mulungu wanu kuti ndalowadi mʼdziko limene Yehova analumbira kwa makolo athu kuti adzatipatsa.’+

4 Ndiyeno wansembeyo azikalandira dengulo mʼmanja mwanu nʼkuliika pafupi ndi guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu. 5 Kenako muzikanena pamaso pa Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Bambo anga anali munthu wongoyendayenda wa Chiaramu*+ ndipo anapita ku Iguputo+ ndi anthu ochepa amʼbanja lawo+ nʼkukakhala kumeneko monga mlendo. Koma ali kumeneko anakhala mtundu waukulu ndi wamphamvu.+ 6 Ndipo Aiguputo anayamba kutizunza komanso kutipondereza, moti ankatigwiritsa ntchito yowawa yaukapolo.+ 7 Choncho tinayamba kufuulira Yehova, Mulungu wa makolo athu, ndipo Yehova anamva mawu athu nʼkuona masautso athu, mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu.+ 8 Pamapeto pake Yehova anatitulutsa mu Iguputo ndi dzanja lamphamvu ndi mkono wotambasula,+ zinthu zochititsa mantha, zizindikiro ndiponso zodabwitsa.+ 9 Ndiyeno anatibweretsa kumalo ano nʼkutipatsa dziko ili, dziko loyenda mkaka ndi uchi.+ 10 Choncho ndabweretsa zipatso zoyambirira mwa zipatso za mʼdziko limene Yehova anandipatsa.’+

Ndipo muzikaziika pamaso pa Yehova Mulungu wanu nʼkugwada pamaso pa Yehova Mulungu wanu. 11 Mukatero muzikasangalala chifukwa cha zabwino zonse zimene Yehova Mulungu wanu wapereka kwa inuyo ndi anthu a mʼnyumba yanu, komanso kwa Mlevi ndi mlendo amene akukhala pakati panu.+

12 Mukamaliza kusonkhanitsa chakhumi+ chonse cha zokolola zanu mʼchaka chachitatu, chaka chopereka chakhumi, muzikapereka chakhumicho kwa Mlevi, mlendo amene akukhala pakati panu, mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye ndipo azidzadya nʼkukhuta mʼmizinda yanu.*+ 13 Kenako muzidzanena pamaso pa Yehova Mulungu wanu kuti, ‘Ndachotsa zinthu zonse zopatulika mʼnyumba mwanga nʼkuzipereka kwa Mlevi, mlendo amene akukhala pakati pathu, mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye,+ mogwirizana ndi zimene munandilamula. Sindinaphwanye kapena kunyalanyaza malamulo anu. 14 Sindinadyeko zina mwa zimenezi pa nthawi imene ndinali pa chisoni,* kapena kutengapo zina mwa zimenezi ndili wodetsedwa, kapena kupereka zina mwa zinthu zimenezi chifukwa cha munthu wakufa. Ndamvera mawu a Yehova Mulungu wanga ndipo ndachita zonse zimene munandilamula. 15 Tsopano yangʼanani pansi kuchokera kumwamba, kumalo anu oyera okhalako, ndipo mudalitse anthu anu Aisiraeli ndi dziko limene mwatipatsa,+ dziko loyenda mkaka ndi uchi,+ mogwirizana ndi zimene munalumbira kwa makolo athu.’+

16 Lero Yehova Mulungu wanu akukulamulani kuti muzitsatira malangizo ndi zigamulo zimenezi. Choncho muzisunga ndi kutsatira zimenezi ndi mtima wanu wonse+ komanso moyo wanu wonse. 17 Lero Yehova wakutsimikizirani kuti adzakhala Mulungu wanu ngati mukuyenda mʼnjira zake ndi kusunga malangizo ake,+ malamulo ake+ ndi zigamulo zake+ ndiponso ngati mukumvera mawu ake. 18 Ndipo lero mwatsimikizira Yehova kuti mudzakhala anthu ake komanso chuma chake chapadera,+ mogwirizana ndi zimene anakulonjezani. Ndiponso mwamutsimikizira kuti mudzasunga malamulo ake onse. 19 Zikadzatero adzakukwezani pamwamba pa mitundu ina yonse imene anapanga.+ Zimenezi zidzachititsa kuti mutamandidwe, mutchuke komanso kuti mulandire ulemerero mukapitiriza kukhala anthu oyera kwa Yehova Mulungu wanu,+ mogwirizana ndi zimene anakulonjezani.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena