Yobu
21 Yobu anayankha kuti:
2 “Mvetserani mwatcheru zimene ndikufuna kunena.
Mukachita zimenezi ndiye kuti munditonthoza.
4 Kodi madandaulo anga akupita kwa munthu?
Zikanakhala choncho, kodi ndikanakhalabe woleza mtima?*
5 Tandiyangʼaneni ndipo mudabwa,
Gwirani pakamwa panu.
6 Ndikaziganizira, zikumandisokoneza,
Ndipo thupi langa lonse likumanjenjemera.
8 Ana awo amakhala nawo limodzi nthawi zonse,
Ndipo amakhala ndi moyo wautali moti amaona zidzukulu zawo.
10 Ngʼombe zawo zamphongo sizilephera kupereka bere.
Ngʼombe zawo zazikazi zimabereka ndipo sizibereka ana akufa.
11 Anyamata awo amathamangira panja ngati nkhosa,
Ndipo ana awo amadumphadumpha.
12 Iwo amaimba pogwiritsa ntchito maseche ndi azeze.
Ndipo amasangalala akamva kulira kwa chitoliro.+
14 Koma iwo amauza Mulungu woona kuti, ‘Tisiyeni!
Sitikufuna kudziwa njira zanu.+
15 Kodi Wamphamvuyonse ndi ndani kuti timutumikire?+
Ndipo kodi tingapindule chiyani ngati titamudziwa?’+
16 Koma ndikudziwa kuti alibe mphamvu zochititsa kuti zinthu ziwayendere bwino pa moyo wawo.+
Zimene anthu oipa amaganiza nʼzosiyana* ndi zimene ndimaganiza.+
17 Kodi nyale ya oipa imazimitsidwa kangati?+
Ndipo tsoka limawagwera kangati?
Kodi Mulungu amawawononga kangati atakwiya?
18 Kodi iwo anayamba akhalapo ngati udzu wouluzika ndi mphepo
Kapena ngati mankhusu* amene amauluzika ndi mphepo yamkuntho?
19 Mulungu adzalanga ana a munthu woipa chifukwa cha zolakwa za bambo awo.
Koma Mulungu amulangenso iyeyo kuti adziwe kulakwa kwake.+
21 Ngati chiwerengero cha masiku a moyo wake chitachepa,*
Sadzasamala zimene zidzachitikire anthu amʼnyumba yake iyeyo atapita.+
22 Kodi pali aliyense amene angaphunzitse Mulungu chilichonse,*+
Pamene Mulunguyo ndi amene amaweruza ngakhale anthu apamwamba?+
23 Munthu wina amafa adakali ndi mphamvu+
Ali pa mtendere komanso wopanda nkhawa,+
24 Ntchafu zake zitafufuma ndi mafuta,
Ndipo mafupa ake ali olimba.*
27 Inetu ndikudziwa bwino zimene mukuganiza,
Ndiponso mapulani amene mukupanga kuti mundichitire zoipa.+
28 Chifukwa mukunena kuti, ‘Kodi nyumba ya munthu wolemekezeka ili kuti,
Nanga tenti imene munthu woipa ankakhala ili kuti?’+
29 Kodi simunafunse anthu apaulendo?
Kodi simunafufuze mosamala zimene amanena,*
30 Zoti munthu woipa amapulumuka pa tsiku la tsoka,
Ndiponso kuti pa tsiku la mkwiyo amapulumutsidwa?
31 Ndi ndani angamuuze pamasomʼpamaso kuti akuyenda njira yoipa,
Ndipo ndi ndani angamubwezere pa zimene wachita?
32 Akadzapita naye kumanda,
Anthu adzachezera pamanda ake.
33 Dothi lamʼchigwa* limene adzamukwirire nalo lidzakhala lotsekemera kwa iye,+
Ndipo anthu onse adzamutsatira*+
Mofanana ndi anthu osawerengeka amene anapita iye asanapite.
34 Ndiye nʼchifukwa chiyani mukunditonthoza ndi mawu osathandiza?+
Ndipo mayankho anu ndi mabodza okhaokha.”