Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w95 5/15 tsamba 8-9
  • Mboni za Yehova Padziko Lonse—Sweden

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mboni za Yehova Padziko Lonse—Sweden
  • Nsanja ya Olonda—1995
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Chifutukuko Chifunikiritsa Nyumba
  • Kuyenda Molowera ku Dziko Latsopano
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Ntchito Yomanga Yomwe Imalemekeza Yehova
    Ufumu wa Mulungu Ukulamulira
  • Mmene Anthu Akuwonjezekera Pakufunika Nyumba Zina Mwamsanga
    Nsanja ya Olonda—2002
  • N’chifukwa Chiyani Timamanga Nyumba za Ufumu Ndipo Timazimanga Bwanji?
    Kodi Ndani Akuchita Chifuniro cha Yehova Masiku Ano?
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—1995
w95 5/15 tsamba 8-9

Mboni za Yehova Padziko Lonse​—Sweden

SWEDEN ali kumbali ya kummaŵa kwa ndomo ya Scandinavia ndipo amakwera kupyola pa Arctic Circle. Iye ali wotchuka chifukwa cha nkhalango zake zobiriŵira nthaŵi zonse, ndiponso nyanja zake ndi mapiri, Sweden ali limodzi la maiko a ku Ulaya a anthu okhalirana patalipatali. Chikhalirechobe, Mboni za Yehova zakhoza kupeza okonda choonadi kumeneko chiyambire kumapeto kwa ma 1800. Tangolingalirani za chitsanzo chaposachedwapa.

Mkazi wina anaphunzira Baibulo ndi Mboni, koma mwamuna wake sanakonde zimenezi. Anauza mkazi wake kuleka kuphunzirako, ndipo mkaziyo anatero. Mwamuna ameneyu ankagwira ntchito m’nyumba yosungiramo zinthu zophikira moŵa. Tsiku lina woyendetsa lole wina anafika panyumbapo ndi mdzukulu wake wamwamuna wazaka khumi. Gogo wachimunayo anapempha mwamunayo kuti ayang’anire mnyamatayo pamene anali kupachira katundu mu lole yake. Kuti ayambe kucheza, mwamunayo anafunsa mnyamatayo kuti anapatsidwa mphatso yotani pa tsiku lake la kubadwa laposachedwapa. Mwamunayo anadabwa pamene mnyamatayo anamuuza kuti iyeyo ndi a m’banja lawo samakondwerera masiku akubadwa chifukwa chakuti ali Mboni za Yehova. Mnyamatayo anamuuzanso kuti amalandira mphatso panthaŵi zina m’chaka ndipo samasoŵa kanthu, popeza kuti ali ndi banja labwino ndi lachikondi kwambiri. Palibe mphatso imene inali yamtengo wapatali kuposa imeneyo, iye anawonjezera motero.

Mnyamatayo anafikanso pamalopo ndi agogo ake aamuna kangapo konse. Panthaŵi iliyonse, mwamunayo anali kufunsa mnyamatayo mafunso ambiri, ndipo iye anachita chidwi kwambiri ndi mmene mnyamatayo ankaperekera mayankho oona ndi olunjika, popanda kukayikira kulikonse. Iye anachitanso chidwi ndi kudziŵa makhalidwe abwino kwa mnyamatayo. Usiku wina mwamunayo ataonerera programu ina ya pa wailesi yakanema imene inasonyeza mikhalidwe yomvetsa chisoni m’dziko, anazindikira kuti anafunikira kupenda zinthu zauzimu mwamphamvu. Iye anaimbira telefoni Mboni yachikazi imene inaphunzira ndi mkazi wake ndi kuipempha kufikanso. Posapita nthaŵi, mwamunayo anali kuchititsidwa phunziro ndi Mboni ina yachimuna ndipo anapita patsogolo mofulumira. Anabatizidwa pa April 10, 1994. Mkazi wake nayenso tsopano ndi wobatizidwa.

Chifutukuko Chifunikiritsa Nyumba

Sweden ndi malo a othaŵa kwawo, ndipo Mboni Zachiswidishi zakhala ndi zotulukapo zabwino m’kulalikira kwawo. M’zochitika zambiri ntchitoyo yachitidwa mwachipambano kwakuti Nyumba Zaufumu zakhala zofunika kuti zithandize pa chifutukukocho. Kuyambira 1986 kukafika 1993, Nyumba Zaufumu 37 zinamangidwa ndi njira yomangira nyumba yofulumira, pamene kuli kwakuti nyumba 8 zinakuzidwa ndi kukonzedwanso. Mu 1994 mokha, Nyumba Zaufumu zisanu ndi ziŵiri zinamangidwa, ndipo zitatu zinakonzedwanso.

Pakali pano, pali mipingo 65 imene ikuyembekezera thandizo la kumanga Nyumba Zaufumu zatsopano kapena kukulitsa kapena kukonzanso zimene ali nazo. Antchito odzifunira 2,500 amathandiza pantchito zomanga zotero, ndipo mipingo imayamikira kwambiri thandizo lawo lachikondilo.

Mbali ya kumpoto kwa Sweden, imene imapyola pa Arctic Circle, nthaŵi zina imatchedwa kuti dziko la dzuŵa la pakati pa usiku. Zimenezi zili choncho chifukwa chakuti mkati mwa mbali ina ya chilimwe dzuŵa silimaloŵa kumeneko. Komabe, mu Sweden monse, kuunika kwa choonadi kukupitirizanso kuŵala kwambiri. Limodzi ndi dalitso la Yehova, kuunika kwauzimu kumeneko sikudzazima koma kudzapitirizabe kuŵaliraŵalirabe.

[Bokosi patsamba 8]

ZIŴERENGERO ZA DZIKOLO

Chaka Chautumiki cha 1994

CHIŴERENGERO CHAPAMWAMBA CHA OCHITIRA UMBONI: 24,246

KUGAŴA: Mboni 1 pa anthu 326

OFIKA PA CHIKHUMBUTSO: 40,372

AVAREJI YA OFALITSA AUPAINIYA: 2,509

AVAREJI YA MAPHUNZIRO A BAIBULO: 11,306

CHIŴERENGERO CHA OBATIZIDWA: 850

CHIŴERENGERO CHA MIPINGO: 358

OFESI YA NTHAMBI: ARBOGA

[Chithunzi patsamba 9]

Ofesi ya nthambi ndi Nyumba ya Beteli ku Arboga

[Chithunzi patsamba 9]

Mboni zoyambirira ku Hjo zinagwiritsira ntchito minibasi iyi kufola gawo la mtunda wa makilomita 5,000 monsemonse

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena