Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w02 8/1 tsamba 8
  • ‘Mawu a Mulungu Ali ndi Mphamvu’

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • ‘Mawu a Mulungu Ali ndi Mphamvu’
  • Nsanja ya Olonda—2002
  • Nkhani Yofanana
  • Chowonadi cha Baibulo “Chimapereka Mphamvu”
    Nsanja ya Olonda—1988
  • ‘Mawu a Mulungu Ndi Amphamvu’
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2017
  • ‘Yehova Ali Ndi Mphamvu Zambiri’
    Yandikirani Yehova
  • Mawu a Mulungu Ali ndi Mphamvu
    Nsanja ya Olonda—1994
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2002
w02 8/1 tsamba 8

Olengeza Ufumu Akusimba

‘Mawu a Mulungu Ali ndi Mphamvu’

ANTHU ambiri pachilumba chotentha cha Jamaica panyanja ya Caribbean amalidziŵa bwino Baibulo. Ndipo Baibulo la King James Version limapezeka pafupifupi m’nyumba iliyonse. Anthu ena adzionera okha kuti “mawu a Mulungu ali amoyo, ndi ochitachita [“amphamvu,” NW].” (Ahebri 4:12) Mphamvu imeneyi imasintha miyoyo ya anthu monga momwe chitsanzo chotsatirachi chikusonyezera.

Mwamuna wina dzina lake Cleveland anali atangofika kunyumba kuchokera kuntchito, pamene wa Mboni za Yehova anafika kudzacheza naye. Atakambirana mfundo zina za m’Malemba, Mboniyo inamusiyira Cleveland buku lothandiza kuphunzira Baibulo lakuti Chidziŵitso Chotsogolera ku Moyo Wosatha. Iye sanadziŵe mmene Mawu a Mulungu angasinthire moyo wake.

Cleveland ankapemphera kwa Mulungu katatu patsiku kuti amuthandize kupeza njira yolondola yomulambirira. Iye anaona kuti makolo ake sanali kulambira m’njira yolondola. Ndiyeno anafufuza zipembedzo zina, koma anakhumudwa nazo kwambiri. Ngakhale anali atamvapo za Mboni za Yehova, iye ankakayikira ngati zingakhale ndi choonadi. Komabe, Cleveland anavomera kuphunzira Baibulo ndi Mboni yomwe inafika kunyumba kwake ija. N’chifukwa chiyani anavomera? Chifukwa chakuti ankafuna kuzisonyeza Mbonizo kuti si zolondola.

Posakhalitsa Cleveland anazindikira kuti khalidwe la chiwerewere lomwe ankachita ndi akazi aŵiri ndi losakondweretsa Mulungu. (1 Akorinto 6:9, 10) Atangophunzira maulendo aŵiri okha, iye analimba mtima kukathetsa ubwenzi wake ndi akaziwo. Ndipo anayamba kupita kumisonkhano yachikristu ku Nyumba ya Ufumu. Koma kupita kumisonkhano kunalinso kovuta.

Cleveland ankaseŵera bwino kwambiri mpira wamiyendo m’timu ya m’deralo, ndipo kupita kumisonkhano kunkamuvuta chifukwa cha maseŵeraŵa. Kodi akanatani? Ngakhale kuti oseŵera anzake, mphunzitsi wa timuyo, ndiponso anzake ena, ankam’limbikitsa kwambiri, Cleveland anaganiza zosiya kuseŵera mpira m’timuyo. Inde, Mawu a Mulungu anali atayamba kugwira ntchito, kumulimbikitsa kuti apindule.

Mphamvu ya Mawu a Mulungu inayamba kuonekeranso pamene Cleveland anayamba kuuza ena zomwe ankaphunzira m’Baibulo. (Machitidwe 1:8) Mapeto ake, anzake aŵiri omwe ankaseŵera nawo mpira anayamba kufika pamisonkhano ya Mboni za Yehova. Cleveland atayenerera kukhala wofalitsa wa uthenga wabwino, anali kusangalala kwambiri ndi utumiki, kuthandiza anthu ena pogwiritsa ntchito Mawu a Mulungu.

Mphamvu ya Mawu a Mulungu inapitiriza kumulimbikitsa Cleveland ndipo m’kupita kwanthaŵi anasonyeza kudzipatulira kwake kwa Yehova mwa kubatizidwa. Tsopano ali ndi mwayi wapadera wochita utumiki wanthaŵi zonse ndiponso ndi mtumiki wotumikira mumpingo.

Ku Jamaica ndiponso padziko lonse, anthu miyandamiyanda azindikira kuti, Mawu a Mulungu ‘alidi amoyo ndiponso amphamvu.’

[Mapu/​Chithunzi patsamba 8]

(Onani m’magazini yeniyeni kuti mumvetse izi)

JAMAICA

[Mawu a Chithunzi]

Mapu ndi dziko: Mountain High Maps® Copyright © 1997 Digital Wisdom, Inc.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena