Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 8/00 tsamba 5-6
  • Kubwereramo Kolemba M’sukulu ya Utumiki Wateokalase

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kubwereramo Kolemba M’sukulu ya Utumiki Wateokalase
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
km 8/00 tsamba 5-6

Kubwereramo Kolemba M’sukulu ya Utumiki Wateokalase

Kubwereramo kolemba mabuku atatsekedwa pankhani zokambidwa m’Sukulu ya Utumiki Wateokalase zogaŵiridwa kuyambira mlungu wa May 1 kufikira August 21, 2000. Gwiritsirani ntchito pepala lina kuti mulembepo mayankho ambiri othekera m’nthaŵi yoperekedwa.

[Tamverani: Mkati mwa kupendaku, gwiritsirani ntchito Baibulo lokha kuyankhira funso lililonse. Magwero a nkhani amene amaikidwa pambuyo pa mafunso n’ngoti mukadzifufuzire. Manambala a tsamba ndi ndime nthaŵi zonse sangasonyezedwe m’magwero onse a mu Nsanja ya Olonda.]

Yankhani kuti Zoona kapena Kunama m’ndemanga zotsatirazi:

1. Yankho la Gideoni pa mawu onyoza a amuna a Efraimu linasonyeza kuleza mtima ndi kudzichepetsa kwake ndipo chotero anathetsa kunyoza kwawo kosayenererako ndi kusungitsa mtendere. (Ower. 8:1-3) [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu]

2. Kunena zoona Manowa ndi mkazi wake anaona woyankhulira waumwini wokhala ndi thupi la munthu wa Mulungu osati Yehova weniweniyo ngakhale kuti iye ananena kuti “taona Mulungu.” (Ower. 13:22) [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w88-CN 5/15 tsa. 23 ndime 4.]

3. Ulosi wa wobwebweta wamizimu wa ku Endori sunakwaniritsidwe m’pang’ono pomwe. (1 Sam. 28:19) [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w79 2/15 tsa. 6.]

4. Nkhani ya Davide ndi Bateseba iyenera kusonyeza makolo kuti khalidwe lawo lingakhudze ana awo kwambiri. (2 Sam. 12:13, 14) [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w86 3/15 tsa. 31.]

5. Oweruza 21:25 amanena za nthaŵi pamene Yehova anasiya mtundu wa Israyeli opanda chitsogozo chilichonse. [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w95-CN 6/15 tsa. 22 ndime 16.]

6. Zifaniziro za akerubi pa likasa la chipangano zinaimira kukhalapo kwa Yehova monga Mfumu, amene ankanenedwa kuti ‘amakhala pakati pa akerubi.’ (1 Sam. 4:4) [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w80 11/1 tsa. 29 ndime 2.]

7. Pamene asilikali a Sauli anadya magazi panthaŵi imene anali pa vuto lalikulu kwambiri ndipo sanalangidwe, zinasonyeza kuti nthaŵi zina pangakhale zifukwa zomveka bwino zomwe munthu angaswere malamulo a Mulungu kwakanthaŵi chabe n’cholinga chopulumutsa moyo wake. (1 Sam. 14:24-35) [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w94-CN 4/15 tsa. 31 ndime 7-9.]

8. Ngakhale kuti ena amagwirizanitsa liwu lakuti “kukopa” ndi kusonkhezera ndiponso machenjera, m’lingaliro labwino liwu limeneli lingagwiritsidwe ntchito kupereka lingaliro la kukhutiritsa maganizo ndi kusintha malingaliro a munthu mwa kukambirana naye mogwira mtima ndi momveka bwino. (2 Tim. 3:14, 15) [w98-CN 5/15 tsa. 21 ndime 4]

9. “Phukusi la amoyo” limasonyeza makonzedwe a Mulungu otetezera ndi opulumutsira, amene akanapindulitsa Davide ngati akanapeŵa milandu yakupha pamaso pa Mulungu. (1 Sam. 25:29) [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w91-CN 6/15 tsa. 14 ndime 3.]

10. Pangano la Ufumu wa Davide, lofotokozedwa pa 2 Samueli 7:16, linachepetsa mzera wa Mbewu kukafika kwa Mesiya ndipo linali chitsimikiziro chakuti wina wa m’banja la Davide akadza kudzalamulira “ku nthaŵi zonse.” [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w89-CN 2/1 tsa. 14 ndime 21—tsa. 15 ndime 22.]

Yankhani mafunso otsatiraŵa:

11. Kodi Salmo 34:18 amatipatsa chitsimikizo chotani? [w98-CN 4/1 tsa. 31 ndime 2]

12. Kodi pamene Yosefe anatchulidwanso kuti Barnaba, zinasonyeza chiyani? (Mac. 4:36) [w98-CN 4/15 tsa. 20 ndime 3, mawu a m’munsi]

13. Kodi n’chifukwa chiyani nkhani ya m’Baibulo imati Eli anapitirizabe kuchitira ulemu ana ake aamuna koposa Yehova? (1 Sam. 2:12, 22-24, 29) [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w96-CN 9/15 tsa. 13 ndime 14.]

14. Kodi mutu wa nkhani ungasankhidwe motani? [sg-CN tsa. 44 ndime 2]

15. Malinga ndi 1 Samueli 1:1-7 kodi ndi chitsanzo chabwino kwambiri chiti chimene chinasonyezedwa ndi banja la Samueli? [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w98-CN 3/1 tsa. 16 ndime 12.]

16. Kodi n’chifukwa chiyani tinganene kuti ‘chuma n’chachinyengo’? (Mat. 13:22) [w98-CN 5/15 tsa. 5 ndime 1]

17. Kodi Yonatani wachikulireyo anasonyeza motani kuti akuzindikira wodzozedwa wa Yehova, Davide, ndipo kodi zimachitira chithunzi chiyani lerolino? (1 Sam. 18:1, 3, 4) [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w89-CN 1/1 mas. 24, 26 ndime 4, 13.]

18. Ngakhale kuti anali “wangwiro ndi woongoka,” kodi buku la Yobu limasonyeza motani kuti zimenezi sizitanthauza kuti Yobu anali wosachimwa? (Yobu 1:8) [w98-CN 5/1 tsa. 31 ndime 1]

19. Kodi mawu akuti “yesetsani” amatanthauzanji? (Luka 13:24) [w98-CN 6/15 tsa. 31 ndime 1, 4]

20. Pamene tikugwira ntchito ndi anthu ena, kodi ndi phunziro labwino lotani limene tiyenera kulikumbukira, lolembedwa pa 2 Sam. 12:26-28? [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w93-CN 12/1 tsa. 19 ndime 19.]

Pezani liwu kapena mawu ofunika kutsiriza ndemanga zotsatirazi:

21. Pamene mukukonzekera nkhani, muyenera kusiya mfundo zimene sizikuthandizira kwenikweni ․․․․․․․ wa nkhani yanu. [sg-CN tsa. 41 ndime 10]

22. Mwa kuchita ntchito yabwino ya kukonzekera gawo lililonse mu Sukulu ya Utumiki Wateokalase, timadzilola ․․․․․․․ ndi pulogalamu imeneyi ya maphunziro yomwe Yehova watipatsa. [sg-CN tsa. 43 ndime 18]

23. Dzina la Mulungu, lakuti Yehova, limatanthauza kuti  ․․․․․․․ ndipo limasonyeza kuti Yehova angakwaniritse ntchito iliyonse imene ikufunika kuti akwaniritse ․․․․․․․ zake. [w98-CN 5/1 tsa. 5 ndime 3]

24. Pangano lofotokozedwa pa 2 Samueli 7:12, 13 ndi ․․․․․․․ . [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w89-CN 2/1 tsa. 14.]

25. Fanizo la Yesu la Msamariya wachifundo limasonyeza kuti munthu wolungamadi ndiye amene samangomvera kokha ․․․․․․․ a Mulungu koma amatsanziranso ․․․․․․․ yake. (Luka 10:29-37) [w98-CN 7/1 tsa. 31 ndime 2]

Sankhani yankho lolondola m’ndemanga zotsatirazi:

26. Munthu amene analemekeza banja lake kwambiri kuposa Mulungu anali (Manowa; Eli; Sauli). (1 Sam. 2:29, 30) [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w87-CN 12/15 tsa. 16 ndime 8.]

27. Nthaŵi ya ulamuliro wa oweruza mu Israyeli inatha pamene (Samueli; Davide; Sauli) anadzozedwa kukhala mfumu ndipo mwamsanga pambuyo pake anagonjetsa ( Aamoni; Amoabu; Afilisti) mothandizidwa ndi Yehova. (1 Sam. 11:6, 11) [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w95-CN 12/15 tsa. 9 ndime 2–tsa. 10 ndime 1.]

28. Anali (mtumwi Paulo; atate wake; amayi ndi agogo ake akazi) amene anatsogolera m’kuphunzitsa Timoteo “malembo opatulika” kufikira pakumuona akukhala mmishonale ndi woyang’anira wabwino kwambiri. (2 Tim. 3:14, 15; Afil. 2:19-22) [w98-CN 5/15 tsa. 8 ndime 3–tsa. 9 ndime 5]

29. Pamene tili m’mavuto, Yehova amatiyembekezera kugwiritsa ntchito (nzeru yathu ya kulingalira; mphamvu zathu zakuthupi; chuma chakudziko) ndipo osati kungom’dikirira kuti atikonzere zinthu. [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onaninso w87-CN 4/15 tsa. 19.]

30. Lamulo la Mulungu pa (kulimbana ndi adani; magazi; kunama) silinganyalanyazidwe panthaŵi yangozi. (1 Sam. 14:31-34) [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onaninso w86 9/1 tsa. 25.]

Gwirizanitsani malemba otsatiraŵa ndi ndemanga zondandalikidwa pansipa:

Ower. 11:30, 31; 1 Sam. 15:22; 30:24, 25; 2 Maf. 6:15-17; Yak. 5:11

31. Yehova amatitsimikizira kuti adzagwiritsa ntchito magulu ake ankhondo a kumwamba kutchinjiriza anthu ake malinga ndi chifuniro chake. [w98-CN 4/15 tsa. 29 ndime 5]

32. Akulu a mu mpingo ali ndi udindo womamatira ku mapangano awo ngakhale kuti nthaŵi zina mapanganowo angakhale opweteka maganizo ndiponso ovuta kuwakwaniritsa. [w99-CN 9/15 tsa. 10 ndime 3-4]

33. Kukhalabe wokhulupirika panthaŵi ya mayesero kumadzetsa mphoto yaikulu kwambiri yochokera kwa Yehova Mulungu. [w98-CN 5/1 tsa. 31 ndime 4]

34. Chikondi chenicheni pa Mulungu chimafuna kumvera malangizo a Mulungu ndipo osati kum’phera nsembe kokha. [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w96-CN 6/15 tsa. 5 ndime 1.]

35. Yehova amayamikira kwambiri anthu amene amatumikira m’maudindo ochirikiza gulu lake lerolino. [Kuŵerenga Baibulo kwa mlungu ndi mlungu; onani w86 9/1 tsa. 28 ndime 4.]

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena