Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb25 July tsamba 2-3
  • July 7-13

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • July 7-13
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
mwb25 July tsamba 2-3

JULY 7-13

MIYAMBO 21

Nyimbo Na. 98 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Mfundo Zothandiza Kuti Banja Lizikhala Losangalala

(10 min.)

Musathamangire kulowa m’banja (Miy 21:5; w03 10/15 4 ¶5)

Muzisonyeza kuti ndinu wodzichepetsa pakakhala kusamvana (Miy 21:2, 4; g 7/08 7 ¶2)

Muzichitirana zinthu moleza mtima komanso mokoma mtima (Miy 21:19; w06 9/15 28 ¶13)

Mwamuna akumvetsera mkazi wake moleza mtima pamene akufotokoza maganizo ake.

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Miy 21:31—Kodi kufotokoza zokhudza hatchi palembali, kukutithandiza bwanji kumvetsa bwino udindo wa Yesu mu ulosi wopezeka pa Chivumbulutso 6:2? (w05 1/15 17 ¶9)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Miy 21:1-18 (th phunziro 5)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(3 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. (lmd phunziro 3 mfundo 3)

5. Ulendo Wobwereza

(4 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. (lmd phunziro 7 mfundo 3)

6. Kufotokoza Zimene Mumakhulupirira

(5 min.) Chitsanzo. Ijwfq nkhani na. 54—Mutu: Kodi a Mboni za Yehova Amaiona Bwanji Nkhani Yothetsa Banja? (lmd phunziro 4 mfundo 3)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 132

7. Muzilemekezana M’banja

(15 min.) Nkhani yokambirana.

Chithunzi cha muvidiyo yakuti “Mungatani Kuti Banja Lanu Lizisangalala: Muzisonyezana Ulemu.” Mlongo wabweretsera mwamuna wake chakumwa pa nthawi imene mwamunayo wakhala pampando ndipo akuwerenga.

Mukakwatirana, mumalonjeza pamaso pa Yehova kuti muzikondana komanso kulemekezana. Choncho mmene mumachitira zinthu ndi mwamuna kapena mkazi wanu zimakhudza ubwenzi wanu ndi Yehova.—Miy 20:25; 1Pe 3:7.

Onerani VIDIYO yakuti Mungatani Kuti Banja Lanu Lizisangalala: Muzisonyezana Ulemu. Kenako funsani mafunso awa:

  • Kodi kusonyeza ulemu kwa mwamuna kapena mkazi wanu n’kofunika bwanji?

  • Kodi ndi zinthu ziti zimene tingafunike kusintha n’cholinga choti tizichita zinthu mwaulemu kwambiri?

  • Kodi ndi mfundo zina ziti za m’Baibulo zimene zingatithandize?

  • Kodi tingasonyeze ulemu kwa mwamuna kapena mkazi wathu m’njira ziti?

  • Kodi tiyenera kumaganizira zinthu ziti zokhudza mwamuna kapena mkazi wathu, nanga n’chifukwa chiyani?

8. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) bt mutu 28 ¶16-22

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 72 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena