Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb25 July tsamba 11-16
  • August 11-17

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • August 11-17
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
mwb25 July tsamba 11-16

AUGUST 11-17

MIYAMBO 26

Nyimbo Na. 88 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Muzipewa “Munthu Wopusa”

(10 min.)

“Munthu wopusa” sayenera kulemekezedwa (Miy 26:1; it-2 729 ¶6)

“Anthu opusa” nthawi zambiri amafunikira chilango champhamvu (Miy 26:3; w87 10/1 19 ¶12)

“Munthu wopusa” amakhala wosadalirika (Miy 26:6; it-2 191 ¶4)


TANTHAUZO: M’Baibulo, mawu akuti “munthu wopusa” amatanthauza munthu amene saganiza bwino ndipo satsatira mfundo zolungama za Mulungu.

M’bale wachinyamata akuchoka molimba mtima pamene pali anzake a m’kalasi omwe akuona zinthu zina pafoni.

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Miy 26:4, 5​—N’chifukwa chiyani tinganene kuti mavesi awiriwa satsutsana? (it-1 846)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Miy 26:1-20 (th phunziro 5)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(3 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Yambani kukambirana pogwiritsa ntchito kapepala. (lmd phunziro 1 mfundo 5)

5. Ulendo Wobwereza

(4 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Pitirizani kukambirana za kapepala komwe munasiya pa ulendo wapita. (lmd phunziro 7 mfundo 4)

6. Kuphunzitsa Anthu

(5 min.) Thandizani wophunzira wanu kukonzekera kudzalalikira wachibale wake. (lmd phunziro 11 mfundo 5)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 94

7. Kuphunzira Baibulo Panokha Kumakupatsani ‘Nzeru Zothandiza kuti Mudzapulumuke’

(15 min.) Nkhani yokambirana.

Zithunzi: 1. Mlongo akuphunzira Baibulo kunyumba kwake. Pa kompyuta yake pakuoneka vidiyo ya m’chinenero chamanja. 2. Pa nthawi yopuma, m’bale akuwerenga Baibulo pogwiritsa ntchito foni yake ndipo waika mahedifoni. 3. Mlongo wachikulire akugwiritsa ntchito “JW Library” pa tabuleti yake. 4. Amayi ndi mwana wawo akugwiritsa ntchito “JW Library” pa misonkhano.

Mtumwi Paulo anakumbutsa Timoteyo kuti aziona kuti malemba oyera omwe anaphunzira kuyambira ali mwana ndi ofunika kwambiri. Malemba amenewa anathandiza Timoteyo kupeza ‘nzeru zomuthandiza kuti adzapulumuke.’ (2Ti 3:15) Chifukwa choti choonadi cha m’Baibulo ndi chamtengo wapatali, Mkhristu aliyense ayenera kumapeza nthawi yowerenga komanso kuphunzira Baibulo. Koma bwanji ngati sitisangalala ndi kuphunzira?

Werengani 1 Petulo 2:2. Kenako funsani mafunso awa:

  • Kodi n’zotheka kuti tizisangalala pophunzira Baibulo?

  • Kodi tingatani kuti ‘tizilakalaka’ Mawu a Mulungu?​—w18.03 29 ¶6

  • Kodi mapulogalamu a pa zipangizo zamakono amene gulu la Yehova limatipatsa, angatithandize bwanji pophunzira Baibulo?

Onerani VIDIYO yakuti Zimene Gulu Lathu Lachita​—Zimene Zingakuthandizeni Mukamagwiritsa Ntchito JW Library. Kenako funsani mafunso awa:

  • Kodi pulogalamu ya JW Library® yakuthandizani bwanji?

  • Kodi ndi zinthu ziti mu pulogalamu ya JW Library® zimene zimakusangalatsani?

  • Kodi ndi zinthu ziti mu pulogalamuyi zimene mukufuna kuphunzira n’kuyamba kuzigwiritsa ntchito?

8. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) lfb mutu 8-9

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 89 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena