Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb25 July tsamba 12-13
  • August 18-24

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • August 18-24
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
mwb25 July tsamba 12-13

AUGUST 18-24

MIYAMBO 27

Nyimbo Na. 102 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Anzathu Abwino Amatithandiza

(10 min.)

Anzathu abwino amatipatsa malangizo molimba mtima (Miy 27:5, 6; w19.09 5 ¶12)

Anzathu abwino akhoza kutithandiza bwino kwambiri kuposa achibale athu (Miy 27:10; it-2 491 ¶3)

Anzathu abwino amatithandiza kukhala anthu abwino (Miy 27:17; w23.09 9 ¶7)

M’bale wachinyamata akuthandiza m’bale wachikulire kulankhula ndi adokotala.

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Miy 27:21—Kodi kutamandidwa kumayesa munthu m’njira yotani? (w06 9/15 19 ¶12)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Miy 27:1-17 (th phunziro 5)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(3 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Lalikirani munthu amene si Mkhristu. (lmd phunziro 6 mfundo 5)

5. Ulendo Wobwereza

(4 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Gwiritsani ntchito vidiyo yopezeka pa Zinthu Zophunzitsira. (lmd phunziro 8 mfundo 3)

6. Nkhani

(5 min.) ijwyp nkhani na. 75—Mutu: Ndingatani Ngati Mnzanga Atandikhumudwitsa? (th phunziro 14)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 109

7. “M’bale Amene Anabadwa Kuti Akuthandize Pakagwa Mavuto”

(15 min.) Nkhani yokambirana.

Yehova anatipatsa abale ndi alongo padziko lonse, ndipo pakati pa anthu amenewa tikhoza kupeza anzathu amene amatikonda. N’zoona kuti tikhoza kumacheza ndi anthu onse mumpingo, koma kodi anzathu apamtima ndi angati? Anthu amakhala mabwenzi apamtima ngati amamvetsetsana, amakhulupirirana, amalankhulana momasuka, amachitira zinthu limodzi komanso amathandizana kuchokera pansi pa mtima. Choncho pamafunika nthawi komanso khama kuti anthu ayambe kugwirizana n’kukhala mabwenzi apamtima.

Werengani Miyambo 17:17. Kenako funsani funso ili:

  • N’chifukwa chiyani tiyenera kukhala ndi mabwenzi apamtima panopa chisautso chachikulu chisanayambe?

Werengani 2 Akorinto 6:12, 13. Kenako funsani funso ili:

  • Kodi kugwiritsa ntchito mfundo za m’mavesiwa kungatithandize bwanji kupeza anzathu?

Zithunzi za muvidiyo yakuti “‘Chilichonse Chili ndi Nthawi Yake’​—Kulimbitsa Ubwenzi ndi Anzathu Kumatenga Nthawi.” Kelvin ndi Ben akhala pa benchi pamalo osewerera mpira ndipo Kelvin akupereka mpira kwa Ben.

Onerani VIDIYO yakuti “Chilichonse Chili ndi Nthawi Yake”—Kulimbitsa Ubwenzi ndi Anzathu Kumatenga Nthawi. Kenako funsani funso ili:

  • Kodi mwaphunzira chiyani zokhudza anzanu kuchokera muvidiyoyi?

Kuti mupeze anzanu, mungayambe ndi kuwamwetulira kapena kuwapatsa moni wansangala, kenako n’kumawasonyeza chidwi. Kuti ubwenziwo ulimbe zimatenga nthawi, choncho muzikhala oleza mtima. Mukamachita zinthu zomwe zingalimbitse ubwenzi wanu ndi anzanu, mukhoza kukhala mabwenzi mpaka kalekale.

8. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) lfb mutu 10-11

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 118 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena