Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w23 September tsamba 32
  • Mfundo Zothandiza Pofufuza

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mfundo Zothandiza Pofufuza
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Zoti Ana Achite
  • Muzigwiritsa Ntchito Webusaiti Yathu mu Utumiki—“Khalani Bwenzi la Yehova”
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2015
  • Gwiritsani Ntchito Webusaiti Yathu Pophunzitsa Ana Anu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Mungapeze Nzeru Zokuthandizani pa JW.ORG
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2022
  • Kulemekezana M’banja
    Galamukani!—2024
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
w23 September tsamba 32

Mfundo Zothandiza Pofufuza

Zoti Ana Achite

Makolo ali ndi udindo waukulu wophunzitsa ana zokhudza Yehova. (Aef. 6:4) Pofuna kuthandiza makolo, gulu la Yehova latulutsa zinthu zambiri monga nkhani, mavidiyo komanso nyimbo. Kodi mungagwiritse ntchito bwanji zinthu zimenezi pophunzitsa ana anu?

  • Pezani zinthu zimene zingathandize. Pa JW. ORG, mungapeze zinthu zonse zimene zafalitsidwa zomwe zingathandize ana, monga mavidiyo komanso zoti ana achite pophunzira.a Kuti mupeze zinthu zimenezi, lembani mawu akuti “Ana” kapena “Achinyamata” pamalo ofufuzira.

  • Sankhani zogwirizana ndi ana anu. Pa zinthu zomwe zaikidwa pansi pa kamutu kakuti “Ana,” mungasankhe zimene zingathandize mwana wanu. Kuti mupeze zinthu zimenezi, fufuzani pamalo akuti, “Zochita pa Kulambira kwa Pabanja.”

  • Muzipeza nthawi yokambirana ndi ana anu. Musamangowasiya kuti azionera mavidiyo kapena kuchita zinthu zina n’cholinga choti angotanganidwa nazo. M’malomwake muzikambirana zinthuzo ndi ana anu kuti muwathandize kukhala pa ubwenzi ndi Yehova.

a Panopa, pa JW Library pali mavidiyo onse okhudza achinyamata, koma pa mbali yakuti “Zochita” pali zochepa.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena