MUNGATANI KUTI MUZIKHALA WOSANGALALA?
Dziwani Zambiri
KODI MUNADZIFUNSAPO KUTI:
Ndingatani kuti banja langa lizisangalala?
Ndingatani kuti ndipeze anzanga abwino komanso kuti ena azindiona kuti ndine munthu wabwino?
Kodi anthu amene anamwalira adzakhalanso ndi moyo?
Kodi mavuto amene timakumana nawowa adzathadi?
Kodi anthu sadzaliwonongeratu dziko lapansili?
Kodi zipembedzo zonse zimathandiza anthu kudziwa Mulungu woona?
KUTI MUPEZE MAYANKHO A MAFUNSOWA KOMANSO ENA
Pitani pawebusaiti yathu ya jw.org yomwe ikupezeka m’zinenero zoposa 900. Pamalowa mukhoza kupeza mfundo zothandiza kwambiri pa nkhani zosiyanasiyana.
Mungapezeponso mavidiyo a anthu osiyanasiyana omwe anayamba kusangalala ataphunzira Baibulo ndipo sakunong’oneza bondo. Ena mwa anthuwa ankagwiritsa ntchito mankhwala osokoneza bongo ndipo ena anali akaidi. Enanso ndi ophunzira kwambiri kuphatikizaponso akatswiri a zasayansi.
Pa jw.org/ny mukhoza kuwerenga kapena kupanga dawunilodi Mabaibulo komanso mabuku ndi magazini osiyanasiyana, kwaulere. Nkhani zina zomwe mungazipeze pawebusaiti ndi izi:
Banja Lanu Likhoza Kukhala Losangalala
Kodi Mungatani Kuti Muzisangalala?
Uthenga Wabwino Wochokera kwa Mulungu