Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 6
  • Mwana Wabwino, ndi Woipa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mwana Wabwino, ndi Woipa
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Anthu Aŵiri a Pachibale Amene Anali ndi Mitima Yosiyana
    Nsanja ya Olonda—2002
  • Kaini Anakwiya Mpaka Anapha M’bale Wake
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Kupereka Nsembe Zovomerezeka kwa Yehova
    Nsanja ya Olonda—1999
  • “Ngakhale kuti Anafa, Iye Akulankhulabe”
    Tsanzirani Chikhulupiriro Chawo
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 6

NKHANI 6

Mwana Wabwino, ndi Woipa

YANG’ANANI Kaini ndi Abele tsopano. Onse akula. Kaini wakhala mlimi. Iye amalima dzinthu ndi zipatso ndi ndiwo zamasamba.

Abele wakhala woweta nkhosa. Iye amakonda kusamalira ana a nkhosa. Iwo amakula kukhala nkhosa zazikulu, ndipo chotero Abele posapita nthawi akukhala ndi gulu la nkhosa loliyang’anira.

Tsiku lina Kaini ndi Abele akudza ndi mphatso kwa Mulungu. Kaini akudza ndi zakudya zimene walima. Abele akudza ndi nkhosa yake yabwino kopambana. Yehova akukondwera ndi Abele ndi mphatso yake. Koma sakukondwera ndi Kaini ndi mphatso yake. Kodi mukudziwa chifukwa chake?

Si ubwino wokha wa mphatso ya Abele koposa ya Kaini. N’chifukwa cha ubwino wa Abele. Amakonda Yehova ndi mbale wake. Koma ngwoipa; samakonda mbale wake.

Mulungu akuuza Kaini kusintha. Koma Kaini sakumvetsera. Iye wakwiya kwambiri chifukwa chakuti Mulungu anakonda kwambiri Abele. Chotero Kaini akuti ‘Tiye tipite kumunda.’ Kumene’ko ali okha, Kaini akumenya Abele. Akum’menya zolimba mpaka kumupha. Kodi izi sizinali zoopsya?

Ngakhale Abele anafa, Mulungu akum’kumbukirabe. Iye anali wabwino, ndipo Yehova samaiwala munthu wabwino wonga iye. Tsiku lina Yehova adzaukitsa Abele. Pa nthawi’yo sadzafa’nso. Adzakhala pa dziko pano kosatha. Kodi sikudzakhala kwabwino kudziwa anthu onga iyeyo?

Koma Mulungu samakondwera ndi anthu onga Kaini. Chotero Kaini atapha mbale wake, Mulungu anam’langa mwakum’thamangitsa kwa abale ake. Atachoka kukakhala kwina, anatenga mmodzi wa alongo ake, nam’kwatira.

Kenako Kaini ndi mkazi wake anabala ana. Ana ena amuna ndi akazi a Adamu anakwatirana, nawo’nso anabala ana. Posakhalitsa panali anthu ambiri pa dziko. Tiyeni tiphunzire za ena a iwo.

Genesis 4:2-26; 1 Yohane 3:11, 12; Yohane 11:25.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena