Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 18
  • Yakobo Amka ku Harana

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yakobo Amka ku Harana
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Yakobo Anaona Zinthu Zauzimu Kukhala Zofunika
    Nsanja ya Olonda—2003
  • Moyo Wawo Unali Wovuta Koma “Anamanga Nyumba ya Isiraeli”
    Nsanja ya Olonda—2007
  • Yakobo ali ndi Banja Lalikulu
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Kodi Yehova Amalidalitsa Liti Khama la Munthu?
    Nsanja ya Olonda—2002
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 18

NKHANI 18

Yakobo Amka ku Harana

KODI mukudziwa amuna awa amene Yakobo akulankhula nawo? Atayenda masiku ambiri, Yakobo anawapeza pafupi ndi chitsime. Iwo anali kuweta nkhosa zao. Yakobo anafunsa kuti: ‘Kwanu n’kuti?’ Iwo anati, ku ‘Harana.’

Yakobo anafunsa kuti, ‘Kodi Labani mumam’dziwa?’

Iwo anayankha kuti, ‘Inde. Uyo, adza apo’yo ndi mwana wake wamkazi Rakele ndi gulu lake la nkhosa.’ Kodi mukuona Rakele akudza chauko’yo?

Pamene Yakobo anaona Rakele ndi nkhosa za malume wake Lebani, anamka nakunkuniza mwala pa chitsime kuti nkhosa zimwe. Ndiyeno Yakobo anapsyompsyona Rakele namuuza kuti iye anali yani. Anali wochititsidwa nthumanzi kwambiri, ndipo anamka kunyumba nauza atate wake Labani.

Labani anali wokondwa kwambiri kuti Yakobo adzakhale naye. Ndipo pamene Yakobo anapempha kuti akwatire Rakele, Labani anakondwa. Komabe, anapempha Yakobo kugwira ntchito m’munda mwake kwa zaka zisanu ndi ziwiri kaamba ka Rakele.

Chifukwa anakonda Rakele kwambiri Yakobo anachita izi. Koma nthawi ya ukwati itakwana, kodi mukudziwa chimene chinachitika?

Labani anapatsa Yakobo mwana wake wamkazi wamkulu Leya m’malo mwa Rakele. Pamene Yakobo anabvomereza kugwirira ntchito Labani zaka zina zisanu ndi ziwiri, anam’patsa’nso Rakele akhale mkazi wake. M’nthawiyo Mulungu analola amuna kukhala ndi akazi oposa mmodzi. Koma tsopano, monga momwe Baibulo likunenera, mwamuna ayenera kukhala ndi mkazi mmodzi yekha.

Genesis 29:1-30.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena