Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 42
  • Bulu Alankhula

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Bulu Alankhula
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Bulu wa Balamu Analankhula
    Zimene Tingaphunzire Munkhani za M’Baibulo
  • Kodi Tikanatani Pakadapanda Abulu?
    Galamukani!—2006
  • Yesu Adza Monga Mfumu
    Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Zimene Zili Mʼbuku la Numeri
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 42

NKHANI 42

Bulu Alankhula

KODI munayamba mwamva kuti bulu analankhula? ‘Ai,’ mungatero. ‘Zinyama sizingalankhule.’ Koma Baibulo limasimba za bulu amene analankhula. Tiyeni tione m’mene zinachitikira.

Aisrayeli atsala pang’ono kulowa m’Kanani. Balaki, mfumu ya Moabu, ikuopa Aisrayeli. Chotero akutumiza munthu wochenjera wochedwa Balamu kukatemberera Aisrayeli. Balaki akulonjeza kupatsa Balamu ndalama zochuluka, chotero Balamu akukwera pa bulu wake namka ulendo wokaonana ndi Balaki.

Yehova sakufuna kuti Balamu atemberere anthu Ake. Chotero akutumiza mngelo wokhala ndi lupanga kukatsekereza Balamu. Balamu sakuona mngelo’yo koma bulu wake akuona. Chotero bulu’yo akuyesa kupewa mngelo’yo ndipo potsiriza akungogona pansi pa mseu. Balamu wapsya mtima kwambiri, ndipo akupanda bulu’yo ndi ndodo.

Kenako Yehova akuchititsa Balamu kumva bulu’yo akulankhula naye. ‘Ndakuchitanji kuti wandipanda katatu?’ akufunsa motero bulu’yo.

‘Wandiputsitsa,’ akutero Balamu. ‘N’kadakhala ndi lupanga n’kadakupha!’

‘Kodi n’dakuchitirapo zotere n’kale lonse?’ akufunsa tero bulu’yo.

Balamu akuyankha kuti, ‘Ai.’

Ndiyeno Yehova akuonetsa Balamu mngelo wokhala ndi lupanga woima pa njira’yo. Mngelo’yo akuti: ‘Wapandiranji bulu wako? Ndabwera kudzatsekereza njira yako, chifukwa suyenera kumka kukatemberera Israyeli. Bulu wako akadapanda kundipatukira, n’kadakukantha, koma sin’kadabvulaza bulu wako.’

Balamu akuti: ‘Ndachimwa. Sindinadziwe kuti mwaima panjira.’ Mngelo’yo akulola Balamu kupita, ndipo iye akupita kukaonana ndi Balaki. Iye akuyesabe kutemberera Israyeli, koma m’malo mwake, Yehova akum’chititsa kudalitsa Israyeli katatu.

Numeri 21:21-35; 22:1-40; 23:1-30; 24:1-25.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena