Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • my nkhani 102
  • Yesu Ali Moyo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Yesu Ali Moyo
  • Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
  • Nkhani Yofanana
  • Manda Opanda Kanthu
    Kumamumvetsera Mphunzitsi Wamkuru’yo
  • Mulungu Anakumbukira Mwana Wake
    Phunzirani kwa Mphunzitsi Waluso
  • M’manda a Yesu Munalibe Kanthu Chifukwa Anali Ataukitsidwa
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • Yesu Ngwamoyo!
    Nsanja ya Olonda—1991
Onani Zambiri
Bukhu Langa la Nkhani za Baibulo
my nkhani 102

NKHANI 102

Yesu Ali Moyo

KODI mukudziwa mkazi ndi amuna awiri’wo? Mkazi’yo ndi Mariya wa Magadala, bwenzi la Yesu. Ndipo amuna obvala zoyera’wo ndiwo angelo. Kachipinda kamene Mariya akuyang’anamo ndiko malo amene mtembo wa Yesu unaikidwamo atafa. Amachedwa manda. Koma tsopano mtembo’wo mulibe! Wautenga ndani? Tiyeni tione.

Yesu atafa, ansembe anati kwa Pilato: ‘Yesu akali moyo anati akaukitsidwa pambuyo pa masiku atatu. Chotero lamulani kuti manda’wo alonderedwe. Kuti ophunzira ake asabe mtembo wake ndi kunena kuti iye waukitsidwa kwa akufa! Pilato akuuza ansembe kutumiza asilikali ankhondo kukalondera manda’wo.

M’mawa kwambiri pa tsiku lachitatu pambuyo pa imfa ya Yesu mngelo wa Yehova mwadzidzidzi akudza. Akuchotsa mwala pa manda’wo. Asilikali’wo akuopa kwambiri kwakuti sakutha kuyenda. Kenako, poyang’ana m’mandamo, mtembo’wo mulibe! Ena a asilikali’wo akumka ku mzinda’wo nauza ansembe. Kodi mukudziwa zimene ansembe oipa’wo akuchita? Akupatsa ndalama asilikali’wo kuti adzinama. ‘Muziti ophunzira ake anadza usiku, tiri mtulo, naba mtembo’wo,’ akutero ansembe’wo.

Pa nthawi’yi, akazi ena okonda Yesu akufika pa mandapo. Ndi odabwa chotani m’mene aliri kupeza mulibemo! Mwadzidzidzi angelo awiri obvala zoyera akutulukira. Iwo akufunsa kuti, ‘Mukufuniranji Yesu pano?’ ‘Iye waukitsidwa. Thamangani mukauze ophunzira ake.’ Ha, akazi’wo akuthamanga’di mofulumira! Koma ali pa njira mwamuna wina akuwaimika. Mukudziwa kuti iye ndani? Ndiye Yesu! Iye akuti, ‘Kauzeni ophunzira anga.’

Akazi’wo atauza ophunzira’wo kuti Yesu ali moyo ndipo iwo amuona, ophunzira zikuwabvuta kuzikhulupirira. Petro ndi Yohane akuthamangira kumanda’ko kukadzionera okha, koma m’mandamo muli pululu! Pamene akuchoka Mariya wa Magadala akutsalira m’mbuyo. Ndi pa nthawi’yi pamene akusuzumiramo naonamo angelo awiri.

Kodi mukudziwa chimene chinachitikira mtembo wa Yesu? Mulungu anauchititsa kuzimiririka. Iye sanaukitsire Yesu ku moyo wa thupi lanyama limene anafa nalo lija. Iye anam’patsa thupi latsopano lauzimu, longa la angelo akumwamba. Koma kuti asonyeze ophunzira ake kuti ali moyo, iye akubvala thupi loti n’kuonedwa ndi anthu, monga momwe tidzaphunzirira.

Mateyu 27:62-66; 28:1-15; Luka 24:1-12; Yohane 20:1-12.

Mafunso

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena