Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gl tsamba 22-23
  • Maufumu Athira Nkhondo Dziko Lolonjezedwa

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Maufumu Athira Nkhondo Dziko Lolonjezedwa
  • ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Ufumu wa Babulo
  • Chikristu Chifalikira Kumayiko Ena
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Anthu a Mulungu Abwerera Kudziko Lawo
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Girisi ndi Roma Akhudza Moyo wa Ayuda
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Mayiko Otchulidwa M’baibulo
    ‘Onani Dziko Lokoma’
Onani Zambiri
‘Onani Dziko Lokoma’
gl tsamba 22-23

Maufumu Athira Nkhondo Dziko Lolonjezedwa

Ufumu wa Babulo ndi Asuri

SAMARIYA, likulu la ufumu wakumpoto wa Israyeli, anagonjetsedwa ndi Asuri m’chaka cha 740 B.C.E. Pamenepo Aisrayeli anayamba kulamulidwa ndi ufumu wankhanzawo. Asuri anali kukhala kumpoto chakumapeto kwa zigwa za Mesopotamiya, kufupi ndi Tigirisi, umodzi wa mitsinje yaikulu m’dera la Fertile Crescent. Nimrode anakhazikitsa midzi ya Nineve ndi Kala yomwe inali yofunika kwambiri kwa Asuri. (Gen. 10:8-12) M’nthaŵi ya ulamuliro wa Salimanezere Wachitatu, Asuri anafalikira chakumadzulo mpaka kudera la madzi ochuluka ndiponso zigawo zachonde kwambiri za Suriya ndi kumpoto kwa Israyeli.

Mu ulamuliro wa Mfumu Tiligati Pilesere Wachitatu (Puli), yotchulidwa m’Baibulo, Asuri anayamba kupondereza Israyeli. Asilikali ake anafikanso kum’mwera kwa Yuda. (2 Maf. 15:19; 16:5-18) M’kupita kwa nthaŵi, Asuri analoŵa mu Yuda ngati “madzi” osefukira, nafika ku likulu lake ku Yerusalemu.—Yes. 8:5-8.

Mfumu ya Asuri Sanakeribu inaloŵerera Yuda m’chaka cha 732 B.C.E. (2 Maf. 18:13, 14) Inalanda midzi 46 ya Yuda kuphatikizapo Lakisi, umene unali pamalo abwino kwambiri pa zankhondo opezeka kuchidikha cha Shefela. Monga mmene mapu akusonyezera, asilikali ake anadzera kum’mwera chakumadzulo kwa Yerusalemu, nazungulira likulu la Yudayo. M’mabuku amene analembamo mbiri yake, Sanakeribu anadzitama kuti anasunga Hezekiya “ngati mbalame m’chikwere,” pamene m’mbiri yawo ya Asuri sanatchulemo n’komwe kuphedwa kwa asilikali a Sanakeribu ndi mngelo wa Mulungu.—2 Maf. 18:17-36; 19:35-37.

Ufumu wa Asuri masiku ake anauthera. Amedi, amene anali kukhala m’dera la mapiri limene panopa ndi Iran, anayamba kumenyana ndi asilikali a Asuri otsalawo. Zimenezi zinapangitsa kuti Asuri aiwale madera ake akumadzulo, amenenso anayamba kumuukira. Panthaŵi imeneyi n’kuti Ababulo atayamba kupeza mphamvu moti analanda mudzi wa Ashuri. M’chaka cha 632 B.C.E., Nineve—“mudzi wa mwazi”—unagonjetsedwa ndi mitundu yogwirizana ya Ababulo, Amedi, ndi Asikuti, omwe anali anthu okonda nkhondo ochokera kumpoto kwa Nyanja Yakuda. Zimenezi zinakwaniritsa maulosi a Nahumu ndi Zefaniya.—Nah. 3:1; Zef. 2:13.

Ufumu wa Asuri unathera ku Harana. Ataukiridwa ndi asilikali amphamvu a Ababulo, Asuri anayesetsa kulimba nayo nkhondo akumayembekezera thandizo lochokera ku Igupto. Komabe paulendo wake wopita kumpoto, Farao-neko anachedwa ku Megido polimbana ndi Yosiya, Mfumu ya Yuda. (2 Maf. 23:29) Mmene Neko amafika ku Harana, munali m’mbuyo mwa alendo, moti anapeza Ufumu wa Asuri utagonjetsedwa kale.

Ufumu wa Babulo

Kodi ndi mudzi uti umene umafika m’maganizo mwanu mukamva mawu akuti “minda yolenjekeka ya maluŵa”? Ndi Babulo, likulu la ulamuliro wamphamvu padziko lonse wodziŵika ndi dzina lomweli umene m’maulosi umaimiridwa ndi mkango wamapiko. (Dan. 7:4) Mudzi umenewu unkadziŵika kwambiri chifukwa cha chuma chake, malonda ake, ndiponso kuthandiza kwake pa kufalikira kwa chipembedzo ndi zokhulupirira nyenyezi. Ufumuwo unali m’madambo a kum’mwera kwa Mesopotamiya pakati pa mitsinje ya Tigirisi ndi Firate. Mtsinje wa Firate unadutsa pakati penipeni pa mudziwu, ndipo chifukwa cha makoma ake zimaoneka zosatheka kuloŵa m’mudziwu.

Ababulo anayambitsa njira zamalonda zodutsa m’chipululu chamiyalacha kumpoto kwa Arabiya. Panthaŵi ina yake, Mfumu Nabonidasi anakakhala ku Tema, atasiya Belisazara akulamulira Babulo.

Babulo anaukira Kanani maulendo atatu. Pambuyo poti Nebukadinezara wagonjetsa Aigupto ku Karikemisi m’chaka cha 625 B.C.E., Ababulo analunjika kum’mwera ku Hamati, kumene anagonjetsanso Aigupto amene anali kubwerera kwawo. Kenako Ababulo anasesa dera lonse lakugombe mpaka kuchigwa cha Igupto, ndipo anagonjetsa Asikeloni mmene amapita kum’mwerako. (2 Maf. 24:7; Yer. 47:5-7) Paulendo umenewu, Yuda anayamba kulamulidwa ndi Babulo.—2 Maf. 24:1.

Mfumu Yehoyakimu ya Yuda inapanduka m’chaka cha 618 B.C.E. Ndiyeno Babulo anatumiza asilikali a mitundu yoyandikana ndi Yuda kuti aononge Yudayo koma asilikali a Babuloyo anazinga ndi kugonjetsa Yerusalemu. Patangopita nthaŵi pang’ono chichitikireni zimenezi, Mfumu Zedekiya inagwirizana ndi ufumu wa Igupto ndipo inaputa Ababulo koopsa moti mkwiyo wawo unayakira Yuda. Kachiŵirinso iwo anaukira Yudayo ndipo anayamba kuwononga midzi yake yonse. (Yer. 34:7) Pamapeto pake, Nebukadinezara anatsogolera asilikali ake ku Yerusalemu, ndipo anagonjetsa mzindawo m’chaka cha 607 B.C.E.—2 Mbiri 36:17-21; Yer. 39:10.

[Bokosi patsamba 23]

MABUKU A M’BAIBULO OLEMBEDWA NTHAŴIYI:

Hoseya

Yesaya

Mika

Miyambo (mbali yake ina)

Zefaniya

Nahumu

Habakuku

Maliro

Obadiya

Ezekieli

1 ndi 2 Mafumu

Yeremiya

[Mapu patsamba 23]

(Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)

Maufumu a Babulo ndi Asuri

Ufumu wa Asuri

B4 Mofi (Nofi)

B4 Zoani

B5 IGUPTO

C2 KUPRO (KITIMU)

C3 Sidoni

C3 Turo

C3 Megido

C3 Samariya

C4 Yerusalemu

C4 Asikeloni

C4 Lakisi

D2 Harana

D2 Karikemesi

D2 Aripadi

D2 Hamati

D3 Ribala

D3 ASURI

D3 Damasiko

E2 Gozani

E2 MESOPOTAMIYA

F2 MINI

F2 ASURI

F2 Khorsabad

F2 Nineve

F2 Kala

F2 Ashuri

F3 BABULO

F3 Babulo

F4 KALDAYO

F4 Ereke

F4 Uri

G3 Susani

G4 ELAMU

Ufumu wa Babulo

C3 Sidoni

C3 Turo

C3 Megido

C3 Samariya

C4 Yerusalemu

C4 Asikeloni

C4 Lakisi

D2 Harana

D2 Karikemesi

D2 Aripadi

D2 Hamati

D3 Ribala

D3 ASURI

D3 Damasiko

D5 Tema

E2 Gozani

E2 MESOPOTAMIYA

E4 ARABIYA

F2 MINI

F2 ASURI

F2 Khorsabad

F2 Nineve

F2 Calah

F2 Ashuri

F3 BABULO

F3 BABULO

F4 KALDAYO

F4 Ereke

F4 Uri

G3 Susani

G4 ELAMU

[Malo ena]

G2 MEDIYA

Njira Zazikulu (Onani m’kabuku kenikeni)

[Nyanja]

B3 Nyanja ya Mediterranean (Nyanja Yaikulu)

C5 Nyanja Yofiira

H1 Nyanja ya Caspian

H5 Nyanja ya Perisiya

[Mitsinje]

B5 Nile

E2 Firate

F3 Tigirisi

[Chithunzi patsamba 22]

Chitunda cha Lakisi

[Chithunzi patsamba 22]

Chifanizo cha Megido wakale

[Chithunzi patsamba 23]

Chithunzi chongoyerekezera minda yolenjekeka ya maluŵa ku Babulo

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena