Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • gl tsamba 24-25
  • Anthu a Mulungu Abwerera Kudziko Lawo

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Anthu a Mulungu Abwerera Kudziko Lawo
  • ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Nkhani Yofanana
  • Girisi ndi Roma Akhudza Moyo wa Ayuda
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Mayiko Otchulidwa M’baibulo
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Maufumu Athira Nkhondo Dziko Lolonjezedwa
    ‘Onani Dziko Lokoma’
  • Medi-Perisiya—Mphamvu Yaikulu ya Dziko Yachinayi m’Mbiri ya Baibulo
    Nsanja ya Olonda—1988
Onani Zambiri
‘Onani Dziko Lokoma’
gl tsamba 24-25

Anthu a Mulungu Abwerera Kudziko Lawo

Ufumu wa Mediya ndi Peresiya

DZIKO lamakono la Iran linazunguliridwa ndi mitandadza ya mapiri akuluakulu aŵiri. Mapiriwo ndi Elburz (kum’mwera kwa Nyanja ya Caspian) ndi Zagros (kum’mwera chakum’maŵa kwake kufupi ndi Nyanja ya Perisiya). Pakati pa mapiriŵa pali zigwa zitalizitali zachonde, ndiponso pali mitsetse yomwe ili ndi mitengo yambiri. M’zigwamu simutentha kapena kuzizira kwambiri, koma madera okwera kwambiri, omwe ndi ouma ndipo amaomba mphepo yambiri, ndi amene amazizira kwadzaoneni m’nyengo yachisanu. Kufupi ndi zigwazi kuli chipululu china komwe sikukhala anthu ambiri. Uku, komwe ndi kum’maŵa kwa Mesopotamiya, n’kumene kunabadwira Ufumu wa Mediya ndi Perisiya.

Amedi ankakhala kumpoto m’mapiriŵa, ngakhale kuti anadzayamba kufalikira ku Armenia ndi ku Kilikiya. Koma Aperisi ankakhala kum’mwera chakumadzulo kwake, kum’maŵa kwa Chigwa cha Tigirisi. Mu ulamuliro wa Koresi, cham’katikati mwa zaka za m’ma 500 B.C.E., maufumu aŵiriŵa anagwirizana n’kupanga ufumu wamphamvu padziko lonse wa Mediya ndi Perisiya.

Koresi analanda Babulo mu 539 B.C.E. Kum’maŵa ufumu wake unafika mpaka ku Indiya. Kumadzulo kwake, ufumuwu unaphatikiza dziko la Igupto ndiponso dziko lomwe tsopano ndi Turkey. Danieli anaufotokoza bwino Ufumu wa Mediya ndi Perisiya poutcha kuti ndi “chimbalangondo” chomwe ‘chinalusira nyama zambiri.’ (Dan. 7:5) Koresi anakhazikitsa ulamuliro woganizira anthu, wololera maganizo awo. Iye anagaŵa ufumuwo m’zigawozigawo. Chigawo chilichonse chinkalamulidwa ndi kalonga yemwe nthaŵi zambiri ankakhala Mperisiya, komano pansi pa kalongayo pankakhala mtsogoleri wa m’deralo amene ankakhala ndi mphamvu ndithu. Mitundu yosiyanasiyana imene inali mu ufumuwo ankailimbikitsa kusunga miyambo yawo ndiponso kupitiriza zipembedzo zawo.

Potsatira mfundo imeneyi, Koresi analola Ayuda kubwerera kwawo kukabwezeretsa kulambira koona ndi kukamanganso Yerusalemu, malinga n’kufotokoza kwa Ezara ndi Nehemiya. Kodi mukuganiza kuti chigulu cha anthu chimenechi chinabwerera podutsa njira yomwe Abrahamu anadutsa yotsata Firate kuloŵera cha ku Karikemisi, kapena mwina anadutsa njira yaifupiko yodutsa ku Tadimori ndi ku Damasiko? Baibulo silinenapo chilichonse. (Onani masamba 6-7.) Patapita nthaŵi ndithu, Ayuda anakakhalanso kumadera ena a ufumuwo, monga ku Matsiriro a Nile ndiponso kumadera ena a kum’mwera kwambiri kwa ufumuwo. Ayuda ambiri ndithu anakhalabe ku Babulo, ndipo mwina n’chifukwa chake mtumwi Petro anadzapita kumeneko patatha zaka mazana ambiri. (1 Pet. 5:13) Inde, Ufumu wa Mediya ndi Perisiya ndiwo unachititsa kuti Ayuda azipezeka m’madera ambiri a maufumu otsatira a Girisi ndi Roma.

Atagonjetsa Babulo, Amedi ndi Aperisi anagwiritsa ntchito mudziwu, umene unali kutentha kwambiri m’chilimwe, monga likulu la boma. Mudzi wa Susani, likulu lakale la Aelamu, unali umodzi mwa midzi yachifumu. Patapita nthaŵi, kumeneku n’komwe Mfumu ya Perisiya, Ahaswero (yemwe mosakayikira anali Sasta Woyamba), inatenga Estere kukhala mkazi wake ndi kulepheretsa chiwembu chofuna kupha anthu a Mulungu mu ufumu wonse waukuluwo. Malikulu ena aŵiri a Amedi ndi Aperisi anali Ecbatana (womwe unali pamalo okwera kwambiri, mamita 1,900 ndipo nyengo yake inali yabwino kwambiri m’chilimwe) ndi Pasagade (womwenso unali pamalo okwera mofanana ndi Ecbatana, ndipo unali makilomita pafupifupi 650 kum’mwera chakum’maŵa kwa Ecbatana).

Kodi ulamuliro wamphamvu padziko lonse umenewu unatha motani? Ufumuwu utafika pachimake penipeni, Amedi ndi Aperisi anafuna kuthetsa kugalukira kumene Agiriki anayambitsa kumalire ake a kumpoto chakumadzulo. Panthaŵiyi n’kuti Girisi ali ndi mizinda yokhala ndi maboma akeake ndipo inkathirana nkhondo kwambiri. Koma mizindayi inagwirizana pofuna kugonjetsa asilikali a Aperisi pankhondo zoopsa zomwe anamenyera ku Maratoni ndi ku Salami. Izi zinayala maziko oti Girisi, monga mtundu umodzi wogwirizana, adzagonjetse Amedi ndi Aperisi.

[Bokosi patsamba 25]

Motsogozedwa ndi Zerubabele, amuna achiisrayeli pafupifupi 50,000 anayenda ulendo wobwerera ku Yerusalemu wa makilomita pakati pa 800 mpaka 1,600 (malinga ndi njira yomwe anadutsa). Iwo anakumana ndi vuto lalikulu la zachuma. Dziko lawo linakhala bwinja kwa zaka 70. Anthu obwererawo anayamba kubwezeretsa kulambira koona mwa kumanganso guwa la nsembe ndi kupereka nsembe kwa Yehova. M’nyengo ya phukutho chaka cha 537 B.C.E., anachita Madyerero a Misasa. (Yer. 25:11; 29:10) Kenako obwererawo anayala maziko a nyumba ya Yehova.

[Bokosi patsamba 25]

MABUKU A M’BAIBULO OLEMBEDWA NTHAŴIYI:

Danieli

Hagai

Zekariya

Estere

Masalmo (mbali yake ina)

1 ndi 2 Mbiri

Ezara

Nehemiya

Malaki

[Mapu patsamba 24]

(Onani m’kabuku kenikeni kuti mumvetse izi)

Ufumu wa Mediya ndi Perisiya

A2 MAKEDONIYA

A2 THIRESI

A4 Kurene

A4 LIBIYA

B2 Bezantiyamu

B2 LIDIYA

B3 Sarde

B4 Mofi (Nofi)

B4 IGUPTO

B5 No-Amoni (Thebesi)

B5 Sevene

C3 KILIKIYA

C3 Tariso

C3 Isase

C3 Karikemesi

C3 Tadimori

C3 ASURI

C3 Sidoni

C3 Damasiko

C3 Turo

C4 Yerusalemu

D2 Phasis

D2 ARMENIA

D3 SURIYA

D3 Nineve

D4 Babulo

E3 MEDIYA

E3 Akimeta (Ecbatana)

E3 HYRCANIA

E4 Susani (Susa)

E4 ELAMU

E4 Pasagade

E4 Pesepoli

E4 PERISIYA

F3 PARTHIA

F4 DRANGIANA

G2 Maracanda (Samarkand)

G3 SOGDIANA

G3 BACTRIA

G3 ARIA

G4 ARACHOSIA

G4 GEDROSIA

H5 INDIYA

[Malo ena]

A2 GIRISI

A3 Maratoni

A3 Atene

A3 Salami

C1 SIKUTI

C4 Elati (Eloti)

C4 Tema

D4 ARABIYA

[Mapiri]

E3 MAPIRI A ELBURZ

E4 MAPIRI A ZAGROS

[Nyanja]

B3 Nyanja ya Mediterranean (Nyanja Yaikulu)

C2 Nyanja Yakuda

C5 Nyanja Yofiira

E2 Nyanja ya Caspian

E4 Nyanja ya Perisiya

[Mitsinje]

B4 Nile

C3 Firate

D3 Tigirisi

H4 Indase

[Chithunzi patsamba 24]

Asilikali a Koresi anadutsa m’Mapiri a Zagros kuti afike ku Babulo

[Chithunzi patsamba 25]

Pamwamba: Chipata cha Mitundu Yonse, ku Pesepoli

[Chithunzi patsamba 25]

Chithunzi Chaching’ono: Manda a Koresi ku Pasagade

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena