Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w94 11/1 tsamba 29
  • Chiŵalo China cha Bungwe Lolamulira

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Chiŵalo China cha Bungwe Lolamulira
  • Nsanja ya Olonda—1994
  • Nkhani Yofanana
  • Kugwirizana ndi Bungwe Lolamulira Lerolino
    Nsanja ya Olonda​—1990
  • Mamembala Atsopano a Bungwe Lolamulira
    Nsanja ya Olonda—2000
  • M’bale Watsopano M’Bungwe Lolamulira
    Nsanja ya Olonda—2013
  • Bambo Anga Anamwalira Koma Ndinapeza Bambo Ena
    Nsanja ya Olonda—2014
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—1994
w94 11/1 tsamba 29

Chiŵalo China cha Bungwe Lolamulira

NDI cholinga cha kuwonjezera antchito m’Bungwe Lolamulira la Mboni za Yehova, kuyambira pa July 1, 1994, chiŵalo china chawonjezedwa pa akulu 11 amene akutumikira tsopano lino. Chiŵalo chatsopanocho ndiye Gerrit Lösch.

Mbale Lösch analoŵa utumiki wanthaŵi yonse pa November 1, 1961, namaliza maphunziro m’kalasi ya 41 ya Sukulu ya Gileadi ya Baibulo ya Watchtower. Anatumikira m’ntchito yadera ndi ya chigawo ku Austria kuyambira 1963 mpaka 1976. Anakwatira mu 1967, ndipo iye ndi mkazi wake, Merete, pambuyo pake anatumikira kwa zaka 14 monga ziŵalo za banja la Beteli la ku Austria ku Vienna. Zaka zinayi zapitazo iwo anasamutsidwira ku malikulu a Sosaite ku Brooklyn, New York, kumene Mbale Lösch wakhala akutumikira m’Maofesi Oyang’anira ndipo monga wothandiza Komiti Yautumiki. Chifukwa cha kuzoloŵera kwake kwambiri munda wa ku Ulaya ndi kudziŵa kwake Chijeremani, Chingelezi, Chiromaniya, ndi Chitaliyana, iye adzathandiza kwambiri pantchito ya Bungwe Lolamulira.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena