Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w95 11/1 tsamba 29
  • Zakudya za m’Bokosi Zichita Umboni

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zakudya za m’Bokosi Zichita Umboni
  • Nsanja ya Olonda—1995
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Kudyera Pamodzi Kungathandize Bwanji Banja Lanu?
    Galamukani!—2010
  • Mabokosi
    Yehova Wabwezeretsa Kulambira Koyera
  • Kupereka Thangato Pakati pa Zowonongeka
    Nsanja ya Olonda—1996
  • Zochitika Padzikoli
    Galamukani!—2011
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—1995
w95 11/1 tsamba 29

Zakudya za m’Bokosi Zichita Umboni

M’MASIKU a pambuyo pa chivomezi ku Kobe, Japan, January wathayu, anthu a kumalo okanthidwawo anali kuvutika kupeza chakudya. Komabe, Mboni za Yehova sizinasoŵe chakudya, chifukwa cha thandizo lachikondi la mabwenzi awo. Kwa masiku aŵiri kapena atatu pambuyo pa chivomezi, mipingo yapafupi inapereka mpunga. Posapita nthaŵi, mabwenzi achifundo anayamba kupereka zakudya za m’mabokosi. Ku mabokosi a zakudyawo, ambiri anamamatizako timapepala tolembapo mawu osonyeza chikondi chawo kwa osoŵawo. Awo amene analandira chakudyacho ananena kuti chakudya chilichonse “chinamveka mchere” chifukwa cha misozi yogwerako imene sanakwanitse kuiletsa pamene anaŵerenga timapepalato.

Mboni za Yehova zinagaŵana zakudyazo ndi osoŵa ena. Mboni ina inali kudya chakudya chake cha masana pamene inali kuyenda pagalimoto ndi mnzake wogwira naye ntchito m’kampani imodzi wosakhala Mboni. Motero anagaŵana naye chakudya cha m’limodzi la mabokosi amene anali atalandira kuchokera ku zoperekedwa za chithandizo.

“Kodi chakudya chamasana cha m’bokosi chimenechi mwachigula kuti?” mnzakeyo anafunsa. Mbaleyo anafotokoza ntchito yachithandizo ya Mboni. “Kwa masiku angapo sindinadye ndiwo za masamba. Ndidzasunga zina ndi kupita nazo kunyumba kwa banja langa,” mwamunayo ananena moyamikira.

Nthaŵi yachitatu pamene izi zinachitika, mwamunayo anapereka ma yen 3,000 (pafupifupi $35, U.S.) kwa Mboniyo ndi kunena kuti: “Ndikudziŵa zochita zanu, motero chonde ndiloleni ndipatse chopereka ku ntchito yanu. Ndiyamikira kwambiri kugaŵana kwanu zakudya ndi ine. Mabwenzi anu onse ndi anthu abwinodi.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena