Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w09 11/1 tsamba 6
  • Bodza Lachitatu: Anthu Onse Abwino Amapita Kumwamba

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Bodza Lachitatu: Anthu Onse Abwino Amapita Kumwamba
  • Nsanja ya Olonda—2009
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi Ndani Amene Amapita Kumwanba, ndipo Nchifukwa Ninji?
    Mungathe Kukhala ndi Moyo Kosatha m’Paradaiso pa Dziko Lapansi
  • Zoona Kapena Zopeka?
    Galamukani!—2007
  • Carici Coona ndi Maziko Ace
    Coonadi Cimene Cimatsogolera ku Moyo Wamuyaya
  • Kodi Kumwamba N’kotani?
    Nsanja ya Olonda—2010
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda—2009
w09 11/1 tsamba 6

Bodza Lachitatu: Anthu Onse Abwino Amapita Kumwamba

Kodi bodzali linayamba bwanji?

Chakumayambiriro kwa m’ma 100 C.E., atumwi a Yesu atatha kufa, anthu ena amene ankatchedwa Abambo a Tchalitchi anayamba kutchuka. Pofotokoza zimene ankaphunzitsa, buku lina limanena kuti: “Mfundo imene ankakonda kuphunzitsa inali yakuti mizimu ya anthu akufa imayeretsedwa ndipo kenako imakalowa kumwamba kukasangalala.”​—New Catholic Encyclopedia (2003), Voliyumu 6, tsamba 687.

Kodi Baibulo limati chiyani?

Limanena kuti: “Osangalala ali iwo amene ali ofatsa, popeza adzalandira dziko lapansi.”​—Mateyo 5:5.

Ngakhale kuti Yesu analonjeza ophunzira ake kuti akupita kumwamba ‘kukawakonzera malo,’ iye sanasonyeze kuti anthu onse olungama amapita kumwamba. (Yohane 3:13; 14:2, 3) Ndiponso, kodi Yesu sanapemphere kuti chifuniro cha Mulungu chichitike “monga kumwamba, chomwechonso pansi pano”? (Mateyo 6:9, 10) Zoona zake n’zakuti pali malo awiri amene anthu olungama angayembekeze kudzakhala. Anthu ochepa adzapita kumwamba kukalamulira ndi Khristu, koma anthu ambiri adzakhala ndi moyo kosatha padziko lino lapansi.​—Chivumbulutso 5:10.

Patapita nthawi, tchalitchi choyambirira chinasiya udindo wake padziko lapansili. Kodi zotsatira zake zinali zotani? Buku lina linati: “Tchalitchichi chinasiya kuyembekezera Ufumu wa Mulungu.” (The New Encyclopædia Britannica) Ndipo pofuna kuti tchalitchichi chikhale ndi mphamvu, chinayamba kulowerera ndale ponyalanyaza malangizo omveka bwino a Yesu akuti otsatira ake ‘sali mbali ya dzikoli.’ (Yohane 15:19; 17:14-16; 18:36) Ndipo mfumu ina yachiroma, dzina lake Kositantini, inalimbikitsa anthu a m’tchalitchichi kusiya zimene ankakhulupirira poyamba, monga nkhani yonena za mmene Mulungu alili.

Yerekezani ndi mavesi awa: Salmo 37:10, 11, 29; Yohane 17:3; 2 Timoteyo 2:11, 12

ZOONA N’ZAKUTI:

Anthu ambiri abwino adzakhala ndi moyo wosatha padziko lapansi kosatha, osati kumwamba

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena