Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 8/01 tsamba 1
  • Ndinu “Choonetsedwa”!

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Ndinu “Choonetsedwa”!
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Nkhani Yofanana
  • Angelo Ndiwo “Mizimu Yotumikira Anthu”
    Nsanja ya Olonda—2009
  • Mmene Angelo Amatikhudzira
    Nsanja ya Olonda—2006
  • Muzitsanzira Angelo Okhulupirika
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2025
  • Angelo—Kodi Amayambukira Moyo Wanu?
    Nsanja ya Olonda—1987
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
km 8/01 tsamba 1

Ndinu “Choonetsedwa”!

1 Mtumwi Paulo analemba kuti: “Takhala ife choonetsedwa ku dziko lapansi, ndi kwa angelo, ndi kwa anthu.” (1 Akor. 4:9) Kodi zimenezi zikutanthauzanji, ndipo kodi ziyenera kutikhudza motani mu utumiki wathu lerolino?

2 Mosakayikira mawu akuti “choonetsedwa” anakumbutsa Akorinto zimene zinkachitika kumapeto kwa maseŵera a Aroma, pamene anthu olakwa asanaphedwe mwankhanza ankawadutsitsa kutsogolo kwa khamu loonerera. Mofananamo, namtindi wa anthu ndi wa angelo unkaona momwe Akristu oyambirira ankazunzikira chifukwa cholalikira Ufumu. (Aheb. 10:32, 33) Kukhulupirika kwawo kunakhudza mitima ya anthu ambiri amene ankaona zimenezi zikuchitika, monga momwe kupirira kwathu kumachitira masiku ano. Kodi ndife choonetsedwa kwa ndani?

3 Ku Dziko Lapansi ndi kwa Anthu: Nthaŵi zina olemba nkhani amalemba zochita za anthu a Yehova. Timayamikira akafalitsa mbiri yabwino ndiponso yoona yokhudza ntchito yathu, koma nthaŵi zina timayembekezanso adani athu kufalitsa mbiri yoipa. Komabe, tipitirize kudzitsimikizira tokha monga atumiki a Mulungu “mwa mbiri yoipa ndi mbiri yabwino.” (2 Akor. 6:4, 8) Anthu oona mtima savutika kuona kuti ndife ophunzira oona a Yesu Kristu.

4 Kwa Angelo: Zolengedwa zauzimu nazonso zimationa. Mdyerekezi ndi ziwanda zake amationerera koma ndi “udani waukulu,” akumafuna kuthetsa ntchito ‘yochitira umboni wa Yesu.’ (Chiv. 12:9, 12, 17) Angelo a Mulungu okhulupirika amaona ndipo amasangalala munthu wochimwa mmodzi akatembenuka. (Luka 15:10) N’zolimbikitsa kuti angelo amaona utumiki wathu monga ntchito yofunika mwachangu ndi yopindulitsa kwambiri imene ikuchitika padziko lapansi masiku ano!—Chiv. 14:6, 7.

5 Mukakumana ndi chitsutso kapena mukaganiza kuti utumiki wanu sukuphula kanthu, muzikumbukira kuti maso a anthu onse ali pa inu. Kupirira kwanu kumanena zambiri. Mapeto ake, “nkhondo [yanu] yabwino ya chikhulupiriro” idzakutheketsani ‘kugwira moyo wosatha.’​—1 Tim. 6:12.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena