Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 8/01 tsamba 4
  • Pulogalamu Yatsopano ya Tsiku la Msonkhano Wapadera

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Pulogalamu Yatsopano ya Tsiku la Msonkhano Wapadera
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
  • Nkhani Yofanana
  • Pulogalamu Yatsopano ya Tsiku la Msonkhano Wapadera
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2000
  • Pulogalamu ya Tsiku la Msonkhano Wapadera wa 2010
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2009
  • Programu Yatsopano ya Tsiku la Msonkhano Wapadera
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
  • Programu Yatsopano ya Msonkhano Wadera
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2001
km 8/01 tsamba 4

Pulogalamu Yatsopano ya Tsiku la Msonkhano Wapadera

Mutu wa pulogalamu ya tsiku la msonkhano wapadera wachaka chautumiki chatsopano uli ndi maziko enieni a m’Malemba: “Gonjerani Mulungu—Kanizani Mdyerekezi.” (Yak. 4:7) Ndi langizotu lamphamvu m’nthaŵi zovuta zino! Kumvera Mulungu kumatiika paudani ndi Satana. Pulogalamuyi idzatithandiza momwe tingalimbire mtima kukana njira za Mdyerekezi zowononga chikhulupiriro. Kodi china mwa chuma chauzimu chimene tikamve kumsonkhano umenewu n’chiti?

Woyang’anira dera adzasonyeza momwe “Kugonjera Mulungu Monga Anthu Okhala m’Banja” kumalimbitsira mabanja kupirira mavuto a dzikoli. Pa tsikuli nkhani yoyamba ya mlendo yamutu wakuti, “Tanthauzo la Kukaniza Mdyerekezi,” idzafotokoza chifukwa chake tifunika kulimba mtima kukana zolinga za Satana zofuna kuwononga uzimu wathu ndiponso mmene tingachitire zimenezi. Nkhani ziŵiri ndi zokhudza kwambiri achinyamata, amene ayeneranso kuchenjera ndi misampha ya Mdyerekezi. Akristu ambiri amene panopo ali achikulire anakana kutsatira zofuna za dziko ali achinyamata. Tikasangalala kumva zina mwa zimene akumana nazo.

Anthu onse afunika kugonjera olamulira. Choncho, nkhani yomaliza ya mlendo idzagogomezera mbali zinayi zimene tikufunika kusonyeza kugonjera Mulungu: (1) kwa akuluakulu a boma, (2) mu mpingo, (3) pantchito yolembedwa, ndiponso (4) m’banja. Ndi pulogalamu yothandizadi kwambiri!

Amene akufuna kubatizidwa patsiku la msonkhano wapadera limeneli auze woyang’anira wotsogolera mwamsanga. Tonse tiike chizindikiro pakalendala yathu pa tsiku la msonkhanowu ndipo tikonzekere kudzakhalapo papulogalamu yonse. Madalitso amene timalandira sadzatha ngati tigonjera Yehova kwamuyaya.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena