Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 5/02 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2010
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zimene Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
Onani Zambiri
Utumiki wathu wa Ufumu—2002
km 5/02 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda May 15

“Kodi mukuganiza kuti n’zotheka kum’dziŵa Mulungu? [Yembekezani ayankhe.] Simungakane kuti n’kovuta kukhulupirira munthu amene sitikum’dziŵa bwino, si choncho kodi? Komatu Baibulo limatilimbikitsa kufunafuna Mulungu. [Ŵerengani Machitidwe 17:27.] Nkhani izi zikusonyeza momwe tingam’dziŵire bwino Mulungu.”

Galamukani! June 8

“Olamulira a mayiko osiyanasiyana ayesa njira izi ndi izi kuti athetse mavuto athu. Njira ina yatsopano imene ayesa ndi ya kudalirana pa zinthu zosiyanasiyana. Mungaŵerenge m’magazini iyi momwe njira imeneyi ikukukhudzirani pakalipano. Mungaŵerengenso za njira imene Baibulo linaneneratu kuti ndi imene idzathetse mavuto padziko lonse.” Ndiyeno ŵerengani Mateyu 6:9, 10.

Nsanja ya Olonda June 1

“Chifukwa cha zimene zikuchitika masiku ano anthu akufunsa chifukwa chake anthu osalakwa amafa msanga. Kodi munalingalirapo chifukwa chake anthu amafa? [Yembekezani ayankhe, ndiyeno pitani pabokosi la patsamba 7.] Ndikhulupirira mungakonde kudziŵa zimene Baibulo limanena pa imodzi mwa mfundo zabodza izi zomwe n’zofala, si choncho kodi?” Ngati n’zotheka ŵerengani lemba limene aika pamenepo.

Galamukani! June 8

“Anthu ambiri amaganiza kuti chipembedzo ndi sayansi siziyendera limodzi. Ena afika poganiza kuti munthu wokonda za sayansi sangakhulupirire Mulungu. Kodi inu mumaganiza bwanji? [Yembekezani ayankhe.] Galamukani! iyi ikufotokoza bwino kwambiri nkhani imeneyi.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena