Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 6/02 tsamba 4
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2004
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
Onani Zambiri
Utumiki wathu wa Ufumu—2002
km 6/02 tsamba 4

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda June 15

“Kodi mukuganiza kuti mavuto ngati aŵa adzathadi? [Ŵerengani mawu mu nkhani yoyambayo onena zimene lipoti lina linanena, ndiyeno yembekezani ayankhe.] Mawu ouziridwa a Mulungu akutitsimikizira kuti mavuto ameneŵa atha posachedwapa. [Ŵerengani Salmo 72:12-14.] Nsanja ya Olonda iyi ikulongosola momwe zimenezi zidzachitikire.”

Galamukani! July 8

“Kodi mukuganiza kuti zidzatheka kuti anthu onse padziko lapansi akhale pa ufulu weniweni? [Yembekezani ayankhe.] Taonani lonjezo labwino ili la Mulungu. [Ŵerengani Aroma 8:21.] Koma kuti zimenezi zichitike, ukapolo uyenera kutha kaye, sichoncho kodi? Galamukani! iyi ikusonyeza momwe zimenezi zidzachitikire.”

Nsanja ya Olonda July 1

“Anthu mamiliyoni ambiri amagwiritsa ntchito mafano kapena zifanizo polambira, ndipo anthu ena mamiliyoni ambiri amaganiza kuti kuchita zimenezi n’kulakwa. Kodi munayamba mwalingalira zimene Mulungu amaganiza pankhaniyi? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani Yohane 4:24.] Nkhani izi zikusonyeza momwe kulambira mogwiritsa ntchito zifaniziro kunayambira ndiponso zimene Baibulo limanena pankhani yolambira mafano.”

Galamukani! July 8

“Baibulo linalosera kuti masiku otsiriza adzakhala ovuta kwambiri. [Ŵerengani 2 Timoteo 3:1, 3.] Kuchuluka kwa upandu padziko lonse ndi umboni wa zimenezi. Zinthu zikanaipa kwambiri pakanakhala kuti palibe apolisi. Galamukani! iyi ikufotokoza mavuto amene apolisi padziko lonse amakumana nawo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena