Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 11/02 tsamba 8
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
  • Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • Nkhani Yofanana
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2006
  • Zomwe Munganene Pogawira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2008
  • Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2003
Onani Zambiri
Utumiki wathu wa Ufumu—2002
km 11/02 tsamba 8

Zomwe Munganene Pogaŵira Magazini

Nsanja ya Olonda Nov. 15

“Anthu ena afunsa ngati matchalitchi ndi akachisi ali ofunika polambira Mulungu. Kodi mukuganiza bwanji? [Yembekezani ayankhe.] Onani zimene Baibulo limanena pankhani imeneyi. [Ŵerengani Machitidwe 17:24.] Choncho, kodi malo olambiriramo ayenera kugwira ntchito yanji? Magazini iyi ikuyankha funso limeneli mogwiritsa ntchito Malemba.”

Galamukani! Nov. 8

“Kodi mumaganiza kuti mapemphero a atsogoleri achipembedzo kapena a munthu wina aliyense angabweretse mtendere padziko lonse? [Yembekezani ayankhe.] Baibulo limalonjeza kuti nthaŵi ina dziko lonse lidzakhala pamtendere. [Ŵerengani Yesaya 9:6, 7.] Kodi mwaona kuti wolamulira winawake wapadera ndiye adzabweretse mtendere padziko lapansili? Galamukani! iyi ikutchula wolamulira ameneyu ndiponso mmene adzabweretsere mtendere weniweni.”

Nsanja ya Olonda Dec. 1

“Masiku ano, pafupifupi aliyense amavutika kuti apeze zinthu zofunika pamoyo. Chimodzimodzinso matchalitchi, ndipo achita kunyanya kupemphetsa ndalama. Kodi zimenezi zimakuvutitsani maganizo? [Yembekezani ayankhe. Ndiyeno ŵerengani 1 Atesalonika 2:9.] Nsanja ya Olonda iyi ikulongosola zimene Baibulo limanena pankhani imeneyi.”

Galamukani! Nov. 8

“Ulosi wa Baibulo umasonyeza kuti ikudza nthaŵi imene padzakhala palibe munthu wonena kuti, ‘Ndikudwala.’ [Ŵerengani Yesaya 33:24.] Kodi sizidzakhala zosangalatsa zimenezi? [Yembekezani ayankhe.] Komabe, masiku ano anthu akuvutika ndi matenda ambiri, ndiponso mliri wa Edzi. Galamukani! iyi ikuyankha funso lakuti, Kodi Edzi idzathetsedwa?”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena