Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 12/02 tsamba 1
  • Lalikirani Uthenga wa Ufumu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Lalikirani Uthenga wa Ufumu
  • Utumiki wathu wa Ufumu—2002
  • Nkhani Yofanana
  • Choonadi Chonena za Ufumu wa Mulungu
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2020
  • Ufumu Umene “Sudzawonongeka”
    Ogwirizana m’Kulambiridwa kwa Mulungu Yekha Wowona
  • Ufumu “Woti Sudzawonongeka ku Nthaŵi Zonse”
    Lambirani Mulungu Woona Yekha
  • Uthenga Umene Tiyenera Kulengeza
    Pindulani ndi Sukulu ya Utumiki wa Mulungu
Onani Zambiri
Utumiki wathu wa Ufumu—2002
km 12/02 tsamba 1

Lalikirani Uthenga wa Ufumu

1 “Kundiyenera Ine ndilalikire Uthenga Wabwino wa Ufumu wa Mulungu . . . chifukwa ndinatumidwa kudzatero.” (Luka 4:43) Ndi mawu ameneŵa, Yesu anasonyeza kuti mfundo yaikulu ya utumiki wake inali Ufumu wa Mulungu. Uthenga umene timalalikira masiku ano wagonanso pa Ufumu, monga momwe Mateyu 24:14 analosera kuti: “Uthenga uwu wabwino wa Ufumu udzalalikidwa padziko lonse lapansi, ukhale mboni kwa anthu a mitundu yonse; ndipo pomwepo chidzafika chimaliziro.” Kodi ndi mfundo ziti za choonadi cha Ufumu wa Mulungu zimene anthu afunika kumva?

2 Ufumu wa Mulungu tsopano ukulamulira kumwamba ndipo posachedwapa udzatenga malo a maulamuliro onse a anthu. Mdyerekezi anathamangitsidwa kale kumwamba, ndipo dziko loipa lino lili m’masiku ake otsiriza. (Chiv. 12:10, 12) Dziko la Satana lakale ndi loipali lidzatheratu, koma Ufumu wa Mulungu sudzagwedezeka. Udzakhala kosatha.—Dan. 2:44; Aheb. 12:28.

3 Ufumu udzachita zinthu zabwino zimene anthu onse okhulupirika amafuna. Udzachotsa mavuto amene amabwera chifukwa cha nkhondo, upandu, kuponderezana ndiponso umphaŵi. (Sal. 46:8, 9; 72:12-14) Anthu onse adzakhala ndi chakudya chambiri. (Sal. 72:16; Yes. 25:6) Matenda ndi kupunduka zidzakhala zinthu zakale. (Yes. 33:24; 35:5, 6) Pamene anthu azidzakhala angwiro, dziko lidzasintha kukhala paradaiso, ndipo anthu adzakhala pamodzi mogwirizana.—Yes. 11:6-9.

4 Timasonyeza kuti tikufuna kukhala nzika za Ufumu wa Mulungu mwa zimene tikuchita panopo. Uthenga wa Ufumu uyenera kukhudza zochita zathu zonse, komanso zolinga zathu ndiponso zinthu zimene timaika patsogolo. Mwachitsanzo, ngakhale kuti tili ndi udindo wopezera banja lathu zinthu zofunika pamoyo, tisalole zinthu zimenezi kutsamwitsa zinthu za Ufumu. (Mat. 13:22; 1 Tim. 5:8) Koma tiyenera kumvera langizo la Yesu lakuti: “Koma muthange mwafuna Ufumu wake ndi chilungamo chake, ndipo zonse zimenezo [zinthu zofunika pamoyo] zidzawonjezedwa kwa inu.”—Mat. 6:33.

5 Anthu akufunika kuti amve uthenga wa Ufumu ndi kuchitapo kanthu nthaŵi isanathe. Tiyenitu tiwathandize kuchita zimenezi mwa ‘kuwakopa ponena za Ufumu wa Mulungu.’—Mac. 19:8.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena