Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 6/13 tsamba 3
  • Fotokozani Nkhani Imodzi, Koma Asiyireni Magazini Awiri

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Fotokozani Nkhani Imodzi, Koma Asiyireni Magazini Awiri
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Nkhani Yofanana
  • Gwiritsirani Ntchito Magazini Athu m’Njira Yabwino Koposa
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1995
  • Gawirani Magazini mu Utumiki Wanu
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2005
  • Kodi Ndi Ndani Amene Angakonde Magazini Awa?
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
  • Tingathe Kuyambitsa Phunziro kwa Anthu Amene Timawapatsa Magazini
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2013
km 6/13 tsamba 3

Fotokozani Nkhani Imodzi, Koma Asiyireni Magazini Awiri

M’magazini athu a Nsanja ya Olonda ndi Galamukani! mumakhala nkhani zosiyanasiyana zomwe anthu ambiri amazikonda. Koma m’malo mofotokozera munthu nkhani zingapo, tingachite bwino kungomufotokozera nkhani imodzi. Ngati timachita chidwi ndi anthu amene tikuwalalikira komanso ngati timakonzekera bwino nkhani zomwe zili m’magazini athu, tingathe kudziwa nkhani mu Nsanja ya Olonda kapena Galamukani! imene mwininyumba angachite nayo chidwi. Mwachitsanzo, ngati tafika pakhomo lina ndipo taona zidole za ana, tingathe kukambirana ndi mwininyumba nkhani yokhudza kulera bwino ana. Ngati tapeza abambo, tikhoza kukambirana nawo nkhani zimene amuna ambiri amachita nazo chidwi, monga zokhudza ulamuliro wabwino. Ngakhale kuti tingakambirane nkhani imodzi ndi mwininyumba, ngati ali wachidwi tingamusiyire magazini onse awiri, Nsanja ya Olonda ndi Galamukani!

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena