Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 June tsamba 3
  • Khulupirira Yehova Ndipo Chita Zabwino

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Khulupirira Yehova Ndipo Chita Zabwino
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Nkhani Yofanana
  • ‘Kondwerani mwa Yehova’
    Nsanja ya Olonda—2003
  • Pangani Yehova Kukhala Chikhulupiriro Chanu
    Nsanja ya Olonda—1988
  • Muzidalira Yehova Pamene Mapeto Akuyandikira
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Kukhulupirira Ena N’kofunika Kwambiri Kuti Munthu Akhale Wosangalala
    Nsanja ya Olonda—2003
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 June tsamba 3

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | MASALIMO 34-37

Khulupirira Yehova Ndipo Chita Zabwino

“Usapse mtima chifukwa cha anthu ochita zoipa”

37:1, 2

  • Musasiye kutumikira Yehova poona kuti anthu oipa zinthu zikuwayendera bwino. M’malo mwake, muziganizira zimene mungachite potumikira Yehova komanso madalitso amene Iye adzakupatseni

“Khulupirira Yehova ndipo chita zabwino”

37:3

  • Muzikhulupirira kuti Yehova angakuthandizeni kuthana ndi mavuto ndiponso nkhawa zanu. Komanso angakuthandizeni kukhalabe okhulupirika

  • Muzigwira mwakhama ntchito yolengeza uthenga wabwino wa Ufumu wa Mulungu

“Sangalala mwa Yehova”

37:4

  • Muzikhala ndi nthawi yowerenga Baibulo ndiponso kusinkhasinkha n’cholinga choti mumudziwe bwino Yehova

“Lola kuti Yehova akutsogolere panjira yako”

37:5, 6

  • Muzikhulupirira ndi mtima wonse kuti Yehova angakuthandizeni kuthana ndi vuto lina lililonse

  • Muzisonyezabe khalidwe labwino anthu akamakutsutsani, kukuzunzani komanso kukunenerani zinthu zabodza

“Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umuyembekezere ndi mtima wako wonse”

37:7-9

  • Muzipewa kuchita zinthu mopupuluma chifukwa zingachititse kuti musamasangalale komanso zingasokoneze ubwenzi wanu ndi Yehova

“Ofatsa adzalandira dziko lapansi”

37:10, 11

  • Yesetsani kukhala ofatsa ndi kuyembekezera Yehova modzichepetsa kuti adzachotse zosalungama zonse zomwe zikukuchitikirani

  • Muzithandiza Akhristu anzanu komanso kulimbikitsa amene ali ndi nkhawa powakumbutsa kuti dziko latsopano lili pafupi kwambiri

Manja a mngelo akuloza Paradaiso padziko lapansi

Ufumu wa Mesiya udzabweretsa madalitso osaneneka

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena