Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb16 August tsamba 8
  • Tidzagwira Ntchito Yapadera Yogawira Nsanja ya Olonda mu September

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Tidzagwira Ntchito Yapadera Yogawira Nsanja ya Olonda mu September
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Nkhani Yofanana
  • Tonthozani Amene ali ndi Chisoni
    Nsanja ya Olonda—2003
  • ‘Tonthozani Anthu Onse Olira’
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Kodi Mulungu Amatilimbikitsa Bwanji?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yogawira)—2016
  • Chitonthozo ndi Chilimbikitso—Ngale za Mbali Zambiri
    Nsanja ya Olonda—1996
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
mwb16 August tsamba 8

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Tidzagwira Ntchito Yapadera Yogawira Nsanja ya Olonda mu September

Nsanja ya Olonda Na. 5 2016 | Kodi ndi Ndani Angatithandize Tikakhala Pamavuto?

Anthu padzikoli akukumana ndi mavuto ambiri ndipo akufunika kuthandizidwa. (Mlal. 4:1) M’mwezi wonse wa September chaka chino, tidzagwira ntchito yapadera yogawira magazini ya Nsanja ya Olonda. Magaziniyi ili ndi nkhani zomwe zingalimbikitse anthu pa mavuto amene akukumana nawo. Tiyeni tidzayesetse kugawira anthu ambiri magazini imeneyi. Popeza tikufuna kudzalankhula ndi anthu pamaso ndi pamaso kuti tiwalimbikitse, tisadzasiye magaziniwa pakhomo lomwe sitinapeze anthu.

ZIMENE TINGANENE

Munganene kuti, “Tonse timakumana ndi mavuto ndipo timafunika kulimbikitsidwa. Koma kodi ndi ndani amene angatithandize tikakhala pamavuto? [Werengeni 2 Akorinto 1:3, 4.] Magaziniyi ikufotokoza mmene Mulungu amatithandizira tikamakumana ndi mavuto.”

Ngati munthuyo akusonyeza kuti akufuna kudziwa zambiri, m’patseni magaziniyo ndipo kenako, . . .

MUONETSENI VIDIYO YAKUTI N’CHIFUKWA CHIYANI TIYENERA KUPHUNZIRA BAIBULO?

Kenako m’pempheni kuti muziphunzira naye Baibulo.

MUFUNSENI FUNSO LIMENE MUDZAKAMBIRANE PA ULENDO WOTSATIRA

Mwachitsanzo mungamufunse kuti, “N’chifukwa chiyani Mulungu amalola kuti anthu azivutika?”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena