Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • yb17 tsamba 128-129
  • Mwamuna Wanga Sankafuna Kusiya Kuwerenga

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mwamuna Wanga Sankafuna Kusiya Kuwerenga
  • Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2017
  • Nkhani Yofanana
  • Kupindula ndi Kuŵerenga Baibulo Tsiku ndi Tsiku
    Nsanja ya Olonda—1995
  • Pamene Amaliŵerenga ndi Mmene Amapindulira
    Nsanja ya Olonda—1995
  • Mungatani Kuti Kuwerenga Baibulo Kuzikuthandizani Kwambiri?
    Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
  • Baibulo—Buku Loyenera Kuŵerengedwa
    Nsanja ya Olonda—1994
Onani Zambiri
Buku Lapachaka la Mboni za Yehova la 2017
yb17 tsamba 128-129

GEORGIA

Mwamuna Wanga Sankafuna Kusiya Kuwerenga

Marina Kopaliani

  • CHAKA CHOBADWA 1957

  • CHAKA CHOBATIZIDWA 1990

  • MBIRI YAKE Marina ndi mwamuna wake Badri, ankachita khama kwambiri pogwira ntchito yolalikira. Ankachita zimenezi ngakhale kuti anali ndi ana awiri. M’kupita kwa nthawi, Badri anatumikira m’Komiti ya Dziko ndipo anakhalabe wokhulupirika mpaka pamene anamwalira mu 2010.

Mlongo Marina Kopaliani

MU 1989, ine ndi mwamuna wanga tinakumana ndi a Mboni za Yehova kunyumba kwa munthu wina yemwe tinayandikana naye nyumba. M’bale Givi Barnadze, yemwe ankaphunzira Baibulo ndi munthuyu, analibe Baibulo lakelake chifukwa pa nthawiyo kukhala ndi Baibulo kunali kovuta kwambiri.

Tinasangalala kwambiri ndi zimene tinamva moti tinaganiza zopeza Baibulo lathulathu. Mwamuna wanga atakumana ndi mchimwene wake anamuuza kuti tikufunitsitsa titapeza Baibulo. Iye anadabwa kwambiri mchimwene wakeyo atamuuza kuti anali atangogula kumene Baibulo latsopano lachijojiya. Anamuuzanso kuti amupatsa Baibulolo ngati mphatso.

Mwamuna wanga atafika kunyumba, anakhala pampando n’kuyamba kuwerenga Baibulo mpaka dzuwa linalowa. Tsiku lotsatira, anapitiriza kuwerenga Baibulo lija. Ndiye madzulo pamene ndinkafika kuchokera kuntchito, ndinamupeza akuwerengabe. Mwamuna wanga sankafuna kusiya kuwerenga. Choncho ndinamuuza kuti atenge tchuthi cha masiku angapo kuti amalize kuwerenga Baibulolo. Anachitadi zimenezi, moti pasanapite nthawi anamaliza kuliwerenga.

Pamene tinayamba kuphunzira Baibulo pogwiritsa ntchito buku la Coonadi Cimene Cimatsogolera ku Moyo Wamuyaya ndi M’bale Barnadze, tinasangalala kwambiri chifukwa tinali ndi Baibulo lathulathu. Zinthu zinayenda bwino, chifukwa ife tinalibe buku la Coonadi, pomwe M’bale Barnadze anali ndi bukuli koma analibe Baibulo. Ndiye ndinganene kuti tinali ndi zinthu zonse zofunika pophunzira Baibulo. Patadutsa pafupifupi chaka, ine ndi mwamuna wanga tinabatizidwa.

Mlongo Marina ndi mwamuna wake
    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena