Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ijwfq nkhani 28
  • Kodi a Mboni za Yehova Amapereka Chakhumi?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kodi a Mboni za Yehova Amapereka Chakhumi?
  • Mafunso Ofunsidwa Kawirikawiri
  • Nkhani Yofanana
  • Kupereka Komwe Kumasangalatsa
    Nsanja ya Olonda—2002
  • Kodi Tingambwezere Motani Yehova?
    Nsanja ya Olonda—1991
  • Kodi Baibulo Limanena Zotani pa Nkhani Yopereka Chakhumi?
    Kuyankha Mafunso a M’Baibulo
  • Kupereka Zoposa Zimene Munthu Angathe
    Nsanja ya Olonda—2002
Onani Zambiri
Mafunso Ofunsidwa Kawirikawiri
ijwfq nkhani 28

Kodi a Mboni za Yehova Amapereka Chakhumi?

Ayi, ife a Mboni za Yehova sitipereka chakhumi. Ndalama zimene zimathandizira kuti ntchito yathu iziyenda bwino ndi zimene anthu, omwe satchulidwa maina, amapereka mwa kufuna kwawo. Kodi chakhumi n’chiyani ndipo n’chifukwa chiyani a Mboni za Yehova sapereka chakhumi?

Lamulo loti anthu azipereka chakhumi, kapena kuti gawo limodzi mwa magawo 10 alionse a zinthu, linali m’gulu la Chilamulo chimene chinaperekedwa kumtundu wakale wa Isiraeli. Komabe, Baibulo limanena momveka bwino kuti Chilamulo, kuphatikizapo lamulo loti anayenera “kulandira zakhumi,” sichikugwira ntchito kwa Akhristu.​—Aheberi 7:​5, 18; Akolose 2:​13, 14.

M’malo mopereka chakhumi ndiponso nsembe, a Mboni za Yehova amatsanzira chitsanzo cha Akhristu oyambirira, omwe ankachita zinthu ziwiri kuti utumiki wawo uziyenda bwino. Choyamba, iwo amagwira ntchito yolalikira popanda kulandira malipiro alionse. Chachiwiri, amapereka mwakufuna kwawo ndalama kapena chuma chawo kuti zithandizire pa ntchitoyi.

Choncho timatsatira malangizo amene ali m’Baibulo, akuti: “Aliyense achite mogwirizana ndi mmene watsimikizira mumtima mwake, osati monyinyirika kapena mokakamizika, chifukwa Mulungu amakonda munthu wopereka mokondwera.”​—2 Akorinto 9:7.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena