12 Abale awo omwe ankagwira ntchito panyumbapo analipo 822. Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu. Yerohamu anali mwana wa Pelaliya, Pelaliya anali mwana wa Amuzi, Amuzi anali mwana wa Zekariya, Zekariya anali mwana wa Pasuri+ ndipo Pasuri anali mwana wa Malikiya.